MIYAMBO 3 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

Malangizo a kuopa, kukhulupirira, ndi kumvera Yehova

1 Deut. 8.1 Mwananga, usaiwale malamulo anga,

mtima wako usunge malangizo anga;

2pakuti adzakuonjezera masiku ambiri,

ndi zaka za moyo ndi mtendere.

3 Deut. 6.8; 2Ako. 3.3 Chifundo ndi choonadi zisakusiye;

uzimange pakhosi pako;

uzilembe pamtima pako;

4 Aro. 14.18 motero udzapeza chisomo ndi nzeru yabwino,

pamaso pa Mulungu ndi anthu.

5 Yer. 9.23 Khulupirira Yehova ndi mtima wako wonse,

osachirikizika pa luntha lako;

6 1Mbi. 28.9 umlemekeze m'njira zako zonse,

ndipo Iye adzaongola mayendedwe ako.

7Usadziyese wekha wanzeru;

opa Yehova, nupatuke pazoipa;

8mitsempha yako idzalandirapo moyo,

ndi mafupa ako uwisi.

9 Eks. 22.29 Lemekeza Yehova ndi chuma chako,

ndi zinthu zako zonse zoyambirira kucha;

10motero nkhokwe zako zidzangoti thee,

mbiya zako zidzasefuka vinyo.

11 Aheb. 12.5-6 Mwananga, usapeputse mwambo wa Yehova,

ngakhale kutopa ndi kudzudzula kwake;

12pakuti Yehova adzudzula omwe awakonda;

monga atate mwana amene akondwera naye.

Phindu la Nzeru

13Wodala ndi wopeza nzeru,

ndi woona luntha;

14 Yob. 28.12-19 pakuti malonda a nzeru aposa malonda a siliva,

phindu lake liposa golide woyengeka.

15 Mat. 13.44 Mtengo wake uposa ngale;

ndipo zonse zikukondweretsa sizilingana naye.

16Masiku ambiri ali m'dzanja lamanja lake;

chuma ndi ulemu m'dzanja lake lamanzere.

17Njira zake zili zokondweretsa,

mayendedwe ake onse ndiwo mtendere.

18 Gen. 2.9; 3.22 Ndiyo mtengo wa moyo wa akuigwira;

wakuiumirira ngwodala.

19Yehova anakhazika dziko ndi nzeru;

naika zamwamba ndi luntha.

20Zakuya zinang'ambika ndi kudziwa kwake;

thambo ligwetsa mame.

21Mwananga, zisachokere kumaso ako;

sunga nzeru yeniyeni ndi kulingalira;

22ndipo mtima wako udzatengapo moyo,

ndi khosi lako chisomo.

23 Mas. 91.11-12 Pompo udzayenda m'njira yako osaopa,

osaphunthwa phazi lako.

24 Lev. 26.6 Ukagona, sudzachita mantha;

udzagona tulo tokondweretsa.

25 Mas. 91.5 Usaope zoopsa zodzidzimutsa,

ngakhale zikadza zopasula oipa;

26pakuti Yehova adzalimbitsa mtima wako,

nadzasunga phazi lako lingakodwe.

Malangizo ena osiyana

27 Aro. 13.7; Agal. 6.10 Oyenera kulandira zabwino usawamane;

pokhoza dzanja lako kuwachitira zabwino.

28 Lev. 19.13 Usanene kwa mnzako, Ukabwerenso,

ndipo mawa ndidzakupatsa;

pokhala uli nako kanthu.

29Usapangire mnzako chiwembu;

popeza akhala nawe pafupi osatekeseka.

30 Aro. 12.18 Usakangane ndi munthu chabe,

ngati sanakuchitire choipa.

31Usachitire nsanje munthu wachiwawa;

usasankhe njira yake iliyonse.

32 Mas. 25.14 Pakuti wamphulupulu anyansa Yehova;

koma chinsinsi chake chili ndi oongoka.

33 Zek. 4.3, 4 Yehova atemberera za m'nyumba ya woipa;

koma adalitsa mokhalamo olungama.

34 1Pet. 5.5 Anyozadi akunyoza,

koma apatsa akufatsa chisomo.

35Anzeru adzalandira ulemu cholowa chao;

koma opusa adzakweza manyazi.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help