1Yehova, imvani pemphero langa,
ndipo mfuu wanga ufikire Inu.
2 Mas. 27.9 Musandibisire nkhope yanu tsiku la nsautso yanga;
munditchereze khutu lanu;
tsiku limene ndiitana ine mundiyankhe msanga.
3Popeza masiku anga akanganuka ngati utsi,
ndi mafupa anga anyeka ngati nkhuni.
4Mtima wanga ukunga udzu womweta, nufota;
popeza ndiiwala kudya mkate wanga.
5Chifukwa cha liu la kubuula kwanga
mnofu wanga umamatika kumafupa anga.
6Ndikunga vuwo m'chipululu;
ndikhala ngati kadzidzi wa kumabwinja.
7Ndidikira, ndikhala ngati mbalame
ili yokha pamwamba pa tsindwi.
8Adani anga anditonza tsiku lonse;
akundiyalukirawo alumbirira ine.
9Pakuti ndadya mapulusa ngati mkate,
ndi kusakaniza chomwera changa ndi misozi,
10 Mas. 30.7 chifukwa cha ukali wanu ndi kuzaza kwanu;
popeza munandinyamula ndipo munandigwetsa.
11 Mas. 109.23; Yes. 40.6-8 Masiku anga akunga mthunzi womka m'tali;
ndipo ine ndauma ngati udzu.
12Koma Inu, Yehova, mukhalabe kunthawi yonse;
ndi chikumbukiro chanu ku mibadwomibadwo.
13 Yes. 60.10 Inu mudzauka, ndi kuchitira nsoni Ziyoni;
popeza yafika nyengo yakumchitira chifundo, nyengo yoikika.
14Pakuti atumiki anu akondwera nayo miyala yake,
nachitira chifundo fumbi lake.
15 1Maf. 8.43 Pamenepo amitundu adzaopa dzina la Yehova,
ndi mafumu onse a dziko lapansi ulemerero wanu.
16 Yes. 60.1-2 Pakuti Yehova anamanga Ziyoni,
anaoneka mu ulemerero wake;
17 Neh. 1.6, 11 anasamalira pemphero la iwo akusowa konse,
osapepula pemphero lao.
18 Aro. 15.4 Ichi adzachilembera mbadwo ukudza;
ndi mtundu wa anthu umene udalengedwa udzamlemekeza Yehova.
19Pakuti anapenya pansi ali kumwamba kuli malo ake opatulika;
Yehova pokhala kumwamba anapenya dziko lapansi;
20 Mas. 79.11 kuti amve kubuula kwa wandende;
namasule ana a imfa.
21 Mas. 22.22 Kuti anthu alalikire dzina la Yehova mu Ziyoni,
ndi chilemekezo chake mu Yerusalemu;
22Posonkhana pamodzi mitundu ya anthu,
ndi maufumu kuti atumikire Yehova.
23Iye analanda mphamvu yanga panjira;
anachepsa masiku anga.
24 Yes. 38.10 Ndinati, Mulungu wanga, musandichotse pakati pa masiku anga:
Zaka zanu zikhalira m'mibadwomibadwo.
25 Gen. 1.1; 2.1; Aheb. 1.10-12 Munakhazika dziko lapansi kalelo;
ndipo zakumwamba ndizo ntchito ya manja anu.
26 Aheb. 1.10-12 Zidzatha izi, koma Inu mukhala:
Inde, zidzatha zonse ngati chovala;
mudzazisintha ngati malaya, ndipo zidzasinthika:
27 Mala. 3.6; Aheb. 13.8 Koma Inu ndinu yemweyo,
ndi zaka zanu sizifikira kutha.
28 Mas. 69.36 Ana a atumiki anu adzakhalitsa,
ndi mbeu zao zidzakhazikika pamaso panu.
Who We AreWhat We EelieveWhat We Do
2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.