2 SAMUELE 22 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

Nyimbo yoyamikira Yehova ya Davide(Mas. 18)

1 Eks. 15.1; Ower. 5.1 Ndipo Davide analankhula kwa Yehova mau a nyimbo iyi tsikuli Yehova anampulumutsa m'dzanja la adani ake onse, ndi m'dzanja la Saulo.

2Deut. 32.4; Mas. 18.2-50Ndipo anati,

Yehova ndiye thanthwe langa,

ndi ngaka yanga, ndi Mpulumutsi wanga, wangadi.

3 Gen. 15.1; Mas. 14.6; Miy. 18.10; Luk. 1.69; Aheb. 2.13 Mulungu wa thanthwe langa,

Iye ndidzamkhulupirira;

chikopa changa, ndi nyanga ya chipulumutso changa,

nsanja yanga yaitali, ndi populumukirapo panga;

Mpulumutsi wanga, mundipulumutsa kuchiwawa.

4Ndidzaitana kwa Yehova amene ayenera timtamande;

chomwecho ndidzapulumutsidwa kwa adani anga.

5 Mas. 32.6 Pakuti mafunde a imfa anandizinga,

mitsinje ya zopanda pake inandiopsa ine.

6Zingwe za kumanda zinandizingira;

misampha ya imfa inandifikira ine.

7 Eks. 3.7; Mas. 116.4 M'kusauka kwanga ndinaitana kwa Yehova,

inde ndinakuwira kwa Mulungu wanga;

ndipo Iye anamva mau anga ali mu Kachisi wake,

ndi kulira kwanga kunafika ku makutu ake.

8Pomwepo dziko linagwedezeka ndi kunthunthumira.

Maziko a dziko la kumwamba anasunthika.

Nagwedezeka, chifukwa Iye anakwiya.

9M'mphuno mwake munatuluka utsi,

ndi moto wotuluka m'kamwa mwake unaononga;

makala anayaka nao.

10Anaweramitsa miyambanso, natsika;

ndipo mdima wandiweyani unali pansi pa mapazi ake.

11Ndipo Iye anaberekeka pa kerubi nauluka;

inde anaoneka pa mapiko a mphepo.

12Ndipo anayesa mdimawo ngati mahema omzungulira Iye,

kusonkhana kwa madzi ndi mitambo yochindikira ya mlengalenga.

13Cheza cha pamaso pake

makala a moto anayaka.

14 Yes. 30.30 Yehova anagunda kumwamba;

ndipo Wam'mwambamwamba ananena mau ake.

15Ndipo Iye anatumiza mivi, nawawaza;

mphezi, nawaopsa.

16Pamenepo m'munsi mwa nyanja munaoneka,

maziko a dziko anaonekera poyera,

ndi mtonzo wa Yehova,

ndi mpumo wa mpweya wa m'mphuno mwake.

17Iye anatumiza kuchokera kumwamba nanditenga;

Iye ananditulutsa m'madzi aakulu.

18Iye anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu,

kwa iwo akudana ndi ine;

pakuti anandiposa mphamvu.

19Anandifikira ine tsiku la tsoka langa;

koma Yehova anali mchirikizo wanga.

20 Mas. 22.8; 31.8 Iye ananditulutsanso ku malo aakulu;

Iye anandipulumutsa,

chifukwa akondwera ndi ine.

21 1Sam. 26.23 Yehova anandibwezera monga mwa cholungama changa;

monga mwa kuyera kwa manja anga anandipatsa mphotho.

22 Mas. 128.1 Pakuti ndinasunga njira za Yehova,

osapatukira ku zoipa kusiya Mulungu wanga.

23Pakuti maweruzo ake onse anali pamaso panga;

ndipo za malemba ake, sindinawapatukire.

24 Yob. 1.1 Ndinakhalanso wangwiro kwa Iye,

ndipo ndinadzisunga kusachita kuipa kwanga.

25 2Sam. 22.21 Chifukwa chake Yehova anandibwezera monga mwa cholungama changa;

monga mwa kuyera kwanga pamaso pake.

26 Mat. 5.7 Ndi chifundo Inu mudzadzionetsa wachifundo,

ndi munthu wangwiro mudzadzionetsa wangwiro.

27 Mas. 24.4; Mat. 5.8 Ndi oyera mtima mudzadzionetsa woyera mtima;

ndi otsutsatsutsa mudzadzionetsa wopotoza.

28 Eks. 3.7-8; Luk. 1.51-52 Ndipo mudzapulumutsa anthu osautsidwa;

koma maso anu ali pa odzikuza kuti muwachepetse.

29Pakuti Inu ndinu nyali yanga, Yehova;

ndipo Yehova adzaunika mumdima mwanga.

30Pakuti ndi Inu ndithamangira gulu;

ndi Mulungu wanga ndilumphira linga.

31 Dan. 4.37; Mat. 5.48 Kunena za Mulungu, njira yake ili yangwiro;

mau a Yehova anayesedwa;

Iye ndiye chikopa kwa onse akukhulupirira Iye.

32Pakuti Mulungu ndani, koma Yehova?

Ndipo thanthwe ndani, koma Mulungu wathu?

33 Mas. 89.26 Mulungu ndiye linga langa lamphamvu;

ndipo Iye ayendetsa angwiro mu njira yake.

34Iye asandutsa mapazi ake akunga mapazi a mbawala;

nandiika pa misanje yanga.

35Iye aphunzitsa manja anga nkhondo;

kotero kuti manja anga alifula uta wamkuwa.

36Ndiponso munandipatsa chikopa cha chipulumutso chanu;

ndi kufatsa kwanu kunandikulitsa.

37Munakulitsa kulunza kwanga pansi panga,

ndi mapazi anga sanaterereke.

38Ndinapirikitsa adani anga, ndi kuwaononga;

ndiponso sindinabwerere mpaka nditawatha.

39Ndinawatha ndi kuwapyoza, kuti sangathe kuuka,

inde anagwa pansi pa mapazi anga.

40Pakuti Inu munandimanga m'chuuno ndi mphamvu ya kunkhondo;

munandigonjetsera akundiukira.

41Munatembenuzitsanso adani anga andipatse mbuyo,

kuti ndiwalikhe akudana ndi ine.

42Anayang'ana iwo, koma panalibe wopulumutsa;

ngakhale kwa Yehova, koma Iye sanawayankhe.

43Pomwepo ndinawasansantha asalale ngati fumbi la padziko,

ndinawapondereza ngati dothi la m'makwalala.

44 Deut. 28.13 Inunso munandipulumutsa ine pa kulimbana kwa anthu anga;

munandisunga ndikhale mutu wa amitundu;

Anthu amene sindinawadziwe adzanditumikira ine.

45Alendo adzandigonjera ine,

pakumva za ine, adzandimvera pomwepo.

46Alendo adzafota,

nadzabwera ndi kunthunthumira otuluka mokwiririka mwao.

47 Eks. 15.2 Yehova ali ndi moyo; ndipo lidalitsike thanthwe langa;

ndipo akulitsidwe Mulungu wa thanthwe la chipulumutso changa;

48inde Mulungu wakundibwezera chilango ine,

ndi kundigonjetsera anthu a mitundu.

49Amene anditulutsa kwa adani anga;

inde mundikweza ine pamwamba pa iwo akundiukira;

mundipulumutsa kwa munthu wachiwawa.

50 Aro. 15.9 Chifukwa chake ndidzakuongani Yehova, pakati pa amitundu,

ndipo ndidzaimba zolemekeza dzina lanu.

51 Mas. 89.20, 29 Iye apatsa mfumu yake chipulumutso chachikulu;

naonetsera chifundo wodzozedwa wake,

kwa Davide ndi mbeu yake ku nthawi zonse.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help