YOBU 17 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

1Mzimu wanga watha, masiku anga afafanizika,

kumanda kwandikonzekeratu.

2Zoonadi, ali nane ondiseka;

ndi diso langa lili chipenyere m'kundiwindula kwao.

3 Miy. 6.1; 17.18 Mupatse chigwiriro tsono,

mundikhalire chikole Inu nokha kwanu;

ndani adzapangana nane kundilipirira?

4Pakuti mwabisira mtima wao nzeru;

chifukwa chake simudzawakuza.

5Iye wakupereka mabwenzi ake ku ukapolo,

m'maso mwa ana ake mudzada.

6Anandiyesanso chitonzo cha anthu;

ndipo ndakhala ngati munthu womthira malovu pankhope pake.

7 Mas. 6.7 M'diso mwanga muchita chizirezire chifukwa cha chisoni,

ndi ziwalo zanga zonse zilibe chithunzi.

8Anthu oongoka mtima adzadabwa nacho,

ndi munthu wosalakwa adzadziutsa kumtsutsa wonyoza Mulunguyo.

9 Mas. 24.4 Koma wolungama asungitsa njira yake,

ndi iye wa manja oyera adzakulabe mumphamvu.

10Koma bwerani inu nonse, idzani tsono;

pakuti sindipeza mwa inu wanzeru.

11Masiku anga apitirira, zolingirira zanga zaduka,

zakezake zomwe za mtima wanga.

12Zisanduliza usiku ukhale usana;

kuunika kuyandikana ndi mdima.

13Ndikayembekezera kumanda kukhale nyumba yanga;

ndikayala pogona panga mumdima.

14Ndikati kwa dzenje, Ndiwe atate wanga;

kwa mphutsi, Ndiwe mai wanga ndi mlongo wanga;

15chilikuti chiyembekezo changa?

Inde, chiyembekezo changa adzachiona ndani?

16Chidzatsikira kumipingiridzo ya kumanda,

pamene tipumulira pamodzi kufumbi.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help