MASALIMO 147 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

Alemekeze dzina la Mulungu chifukwa cha zokoma amachitira anthu ake

1 Mas. 92.1 Aleluya; Pakuti kuimbira zomlemekeza Mulungu wathu nkokoma;

pakuti chikondweretsa ichi, chilemekezo chiyenera.

2 Deut. 30.3; Yes. 11.12 Yehova amanga Yerusalemu;

asokolotsa otayika a Israele.

3 Yes. 57.15; 61.1 Achiritsa osweka mtima,

namanga mabala ao.

4 Yes. 40.26 Awerenga nyenyezi momwe zili;

azitcha maina zonsezi.

5 Yes. 40.28 Ambuye wathu ndi wamkulu ndi wa mphamvu zambiri;

nzeru yake njosatha.

6 Mas. 146.8-9 Yehova agwiriziza ofatsa;

atsitsira oipa pansi.

7Yamikani Yehova ndi kuthira mang'ombe;

muimbireni Mulungu wathu zomlemekeza pazeze:

8Amene aphimba thambo ndi mitambo,

amene akonzera mvula nthaka,

amene aphukitsa msipu pamapiri.

9 Mas. 145.15; Mat. 6.26 Amene apatsa zoweta chakudya chao,

ana a khwangwala alikulira.

10 Hos. 1.7 Mphamvu ya kavalo siimkonda:

Sakondwera nayo miyendo ya munthu.

11Yehova akondwera nao akumuopa Iye,

iwo akuyembekeza chifundo chake.

12Yerusalemu, lemekezani Yehova;

Ziyoni, lemekezani Mulungu wanu.

13Popeza analimbitsa mipiringidzo ya zitseko zanu:

Anadalitsa ana anu m'kati mwanu.

14 Deut. 32.13-14; Yes. 60.17-18 Ndiye amene akhalitsa malire anu mumtendere;

akukhutitsani ndi tirigu wakucha bwino.

15Atumiza lamulo lake kudziko lapansi;

mau ake athamanga liwiro.

16Apatsa chipale chofewa ngati ubweya;

awaza chisanu ngati phulusa.

17Aponya matalala ake ngati zidutsu:

Adzaima ndani pa kuzizira kwake?

18Atumiza mau ake nazisungunula;

aombetsa mphepo yake, ayenda madzi ake.

19Aonetsa mau ake kwa Yakobo;

malemba ake, ndi maweruzo ake kwa Israele.

20 Aro. 3.1-2 Sanatero nao anthu a mtundu wina;

ndipo za maweruzo ake, sanawadziwe.

Aleluya.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help