MASALIMO 96 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

Onse a pansi pano ndi am'mwamba omwe alemekeze Mulungu(1Mbi. 16.23-33)

1 Mas. 33.3 Muimbireni Yehova nyimbo yatsopano;

muimbireni Yehova, inu, dziko lonse lapansi.

2Muimbireni Yehova, lemekezani dzina lake;

lalikirani chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.

3Fotokozerani ulemerero wake mwa amitundu;

zodabwitsa zake mwa mitundu yonse ya anthu.

4 Mas. 95.3 Pakuti Yehova ndi wamkulu, nayenera kulemekezedwa kwakukulu;

ayenera amuope koposa milungu yonse.

5Pakuti milungu yonse ya mitundu ya anthu ndiyo mafano,

koma Yehova analenga zakumwamba.

6 Mas. 29.1-2 Pamaso pake pali ulemu ndi ukulu.

M'malo opatulika mwake muli mphamvu ndi zochititsa kaso.

7Mpatseni Yehova, inu, mafuko a mitundu ya anthu,

mpatseni Yehova ulemerero ndi mphamvu.

8Mpatseni Yehova ulemerero wa dzina lake;

bwerani nacho chopereka, ndipo fikani kumabwalo ake.

9 Mas. 29.1-2 Gwadirani Yehova moyera ndi mokometsetsa,

njenjemerani pamaso pake, inu dziko lonse lapansi.

10 Mas. 93.1 Nenani mwa amitundu, Yehova achita ufumu;

dziko lokhalamo anthu lomwe likhazikika kuti silingagwedezeke;

adzaweruza mitundu ya anthu molunjika.

11 Mas. 69.34 Kumwamba kukondwere nilisekerere dziko lapansi;

nyanja ibume mwa kudzala kwake.

12Munda ukondwerere ndi zonse zili m'mwemo;

pamenepo mitengo yonse ya kunkhalango idzafuula mokondwera.

13 Mas. 67.4 Pamaso pa Yehova, pakuti akudza;

pakuti akudza kudzaweruza dziko lapansi

Adzaweruza dziko lokhalamo anthu ndi chilungamo,

ndi mitundu ya anthu ndi choonadi.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help