MASALIMO 64 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

Davide apempha Mulungu amtchinjirize pa omlaliraKwa Mkulu wa Nyimbo. Salimo la Davide.

1Imvani Mulungu, mau anga, m'kudandaula kwanga;

sungani moyo wanga angandiopse mdani.

2Ndibiseni pa upo wachinsinsi wa ochita zoipa;

pa phokoso la ochita zopanda pake.

3Amene anola lilime lao ngati lupanga,

napiringidza mivi yao, ndiyo mau akuwawitsa;

4kuponyera wangwiro mobisika:

Amponyera modzidzimutsa, osaopa.

5 Miy. 1.11 Alimbikitsana m'chinthu choipa;

apangana za kutchera misampha mobisika;

akuti, Adzaiona ndani?

6Afunafuna zosalungama; kusanthula, asanthuladi mpaka kutha;

chingakhale cha m'kati mwake mwa munthu, ndi mtima wozama.

7Koma Mulungu adzawaponyera muvi;

adzalaswa modzidzimutsa.

8 Miy. 18.7 Adzawakhumudwitsa, lilime lao lidzawatsutsa;

onse akuwaona adzawathawa.

9 Yer. 51.10 Ndipo anthu onse adzachita mantha;

nadzabukitsa chochita Mulungu,

nadzasamalira ntchito yake.

10 Mas. 32.11 Wolungama adzakondwera mwa Yehova,

nadzakhulupirira Iye;

ndipo oongoka mtima onse adzalemekeza.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help