MASALIMO 77 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

Achita nkhawa pokumbuka zochita Mulungu, koma alimbika mtima pokumbuka zina adazichita IyeKwa Mkulu wa Nyimbo: pa Yedutuni. Salimo la Asafu.

1Ndidzafuulira kwa Mulungu ndi mau anga;

kwa Mulungu ndi mau anga, ndipo adzanditcherezera khutu.

2 Mas. 50.15 Tsiku la nsautso yanga ndinafuna Ambuye.

Dzanja langa linatambalika usiku, losaleka;

mtima wanga unakana kutonthozedwa.

3Ndikumbukira Mulungu ndipo ndivutika;

ndilingalira ndipo mzimu wanga ukomoka.

4Mundikhalitsa maso;

ndigwidwa mtima wosanena kanthu.

5 Deut. 32.7 Ndinaganizira masiku akale,

zaka zakalekale.

6 Mas. 42.8; Mali. 3.40 Ndikumbukira nyimbo yanga usiku;

ndilingalira mumtima mwanga;

mzimu wanga unasanthula.

7 Mas. 74.1 Kodi Ambuye adzataya nthawi yonse?

Osabwerezanso kukondwera nafe.

8 Aro. 9.6 Chifundo chake chalekeka konsekonse kodi?

Lonjezano lake lidatha kodi ku mibadwo yonse?

9 Yes. 49.15 Kodi Mulungu waiwala kuchita chifundo?

Watsekereza kodi nsoni zokoma zake mumkwiyo?

10Ndipo ndinati, Chindiwawa ichi;

koma ndikumbukira zaka za dzanja lamanja la Wam'mwambamwamba.

11 Mas. 143.5 Ndidzakumbukira zimene adazichita Yehova;

inde, ndidzakumbukira zodabwitsa zanu zoyambira kale.

12Ndipo ndidzalingalira ntchito yanu yonse,

ndi kulingalirabe zimene munazichita Inu.

13Mulungu, m'malo opatulika muli njira yanu;

Mulungu wamkulu ndani monga Mulungu?

14Inu ndinu Mulungu wakuchita chodabwitsa;

munazindikiritsa mphamvu yanu mwa mitundu ya anthu.

15 Eks. 6.6 Munaombola anthu anu ndi mkono wanu,

ndiwo ana a Yakobo, ndi a Yosefe.

16 Eks. 14.21 Madziwo anakuonani Mulungu;

anakuonani madziwo; anachita mantha,

zozama zomwe zinanjenjemera.

17Makongwa anatsanula madzi;

thambo lidamvetsa liu lake;

mivi yanu yomwe inatulukira.

18Liu la bingu lanu linatengezanatengezana;

mphezi zinaunikira ponse pali anthu;

dziko lapansi linanjenjemera ndi kugwedezeka.

19 Hab. 3.15 Njira yanu inali m'nyanja,

koyenda Inu nkumadzi aakulu,

ndipo mapazi anu sanadziwike.

20 Eks. 13.21; Yes. 63.11-12 Munatsogolera anthu anu ngati gulu la nkhosa,

ndi dzanja la Mose ndi Aroni.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help