YOWELE Mau Oyamba - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

Mau OyambaYowele adalalikira makamaka pa nthawi ya ufumu wa Persiya, koma za moyo wake sitidziwa bwino. Iye akamba za mliri wa dzombe ndi chilala; zimene zaonongeratu mbeu zonse ndi mitengo yomwe. Mneneriyu aona ngati ichi ndi chizindikiro chosonyeza kuti tsiku la Yehova lidzabwera pamene Mulungu adzalanga anthu onse okana malamulo ake. Tsono Yowele akuwapempha anthuwo kuti atembenuke mtima ndi kubwerera kwa Chauta, poyembekeza kuti mwina Mulungu adzawakhulukira ndi kuwadalitsa monga adawalonjezera. Mau ena odziwika ndi akuti lidzafika tsiku pamene Yehova adzatuma mzimu wake pa anthu onse, aamuna ndi aakazi, achikulire ndi achinyamata omwe.Za mkatimuMliri wa dzombe 1.1—2.17

Lonjezo la kukonzedwanso kwa zinthu 2.18-27

Tsiku la Ambuye 2.28—3.21

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help