MASALIMO 13 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

Munkhawa athawira Mulungu namkhulupiriraKwa Mkulu wa Nyimbo. Salimo la Davide.

1 Deut. 31.17; Mas. 44.24 Mudzandiiwala chiiwalire, Yehova, kufikira liti?

Mudzandibisira ine nkhope yanu kufikira liti?

2Ndidzachita uphungu m'moyo mwanga kufikira liti,

pokhala ndi chisoni m'mtima mwanga tsiku lonse?

Adzandiukira ine mdani wanga kufikira liti?

3 Ezr. 9.8 Penyani, ndiyankheni, Yehova Mulungu wanga.

Penyetsani maso anga, kuti ndingagone tulo ta imfa;

4 Mas. 25.2 kuti anganene mdani wanga, Ndamgonjetsa;

ndipo angakondwere otsutsana nane posunthika ine.

5 Mas. 33.21 Koma ine ndakhulupirira pa chifundo chanu;

mtima wanga udzakondwera nacho chipulumutso chanu.

6 Mas. 116.7 Ndidzaimbira Yehova,

pakuti anandichitira zokoma.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help