1 Aleluya; Lemekezani dzina la Yehova!
Lemekezani inu atumiki a Yehova.
2 Luk. 2.37 Inu akuimirira m'nyumba ya Yehova,
m'mabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.
3 Mas. 119.68 Lemekezani Yehova; pakuti Yehova ndiye wabwino;
muimbire zolemekeza dzina lake; pakuti nkokondweretsa kutero.
4 Eks. 19.5 Pakuti Yehova anadzisankhira Yakobo,
Israele, akhale chuma chake chenicheni.
5Pakuti ndidziwa kuti Yehova ndi wamkulu,
ndi Ambuye wathu aposa milungu yonse.
6 Mas. 115.3 Chilichonse chimkonda Yehova achichita,
kumwamba ndi padziko lapansi, m'nyanja ndi mozama monse.
7Akweza mitambo ichokere ku malekezero a dziko lapansi;
ang'animitsa mphezi zidzetse mvula;
atulutsa mphepo mosungira mwake.
8 Eks. 12.12, 29 Anapanda oyamba a Ejipito,
kuyambira munthu kufikira zoweta.
9 Eks. 7.10 Anatumiza zizindikiro ndi zodabwitsa pakati pako, Ejipito iwe,
pa Farao ndi pa omtumikira onse.
10 Num. 21.24-35 Ndiye amene anapanda amitundu ambiri,
napha mafumu amphamvu;
11Sihoni mfumu ya Aamori,
ndi Ogi mfumu ya Basani,
ndi maufumu onse a Kanani:
12Ndipo anapereka dziko lao likhale cholowa,
cholowa cha kwa Israele anthu ake.
13 Eks. 3.15 Dzina lanu, Yehova, likhala kosatha;
chikumbukiro chanu, Yehova, kufikira mibadwomibadwo.
14 Deut. 32.36 Pakuti Yehova adzaweruza anthu ake,
koma adzaleka atumiki ake.
15 Mas. 115.4-10 Mafano a amitundu ndiwo siliva ndi golide,
ntchito ya manja a anthu.
16Pakamwa ali napo koma osalankhula;
maso ali nao, koma osapenya;
17makutu ali nao, koma osamva;
inde, pakamwa pao palibe mpweya.
18Akuwapanga adzafanana nao;
inde, onse akuwakhulupirira.
19A nyumba ya Israele inu, lemekezani Yehova:
A nyumba ya Aroni inu, lemekezani Yehova:
20A nyumba ya Levi inu, lemekezani Yehova:
Inu akuopa Yehova, lemekezani Yehova.
21Alemekezedwe Yehova kuchokera mu Ziyoni,
amene akhala mu Yerusalemu.
Aleluya.
Who We AreWhat We EelieveWhat We Do
2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.