MASALIMO 51 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

Davide avomereza kuchimwa kwake, apempha Mulungu amkhululukire, asamchotsere Mzimu WoyeraKwa Mkulu wa Nyimbo. Salimo la Davide; m'mene anamdzera Natani mneneriyo atalowa iye kwa Bateseba.

1 Yes. 43.25; 44.22; Akol. 2.14 Mundichitire ine chifundo, Mulungu,

monga mwa kukoma mtima kwanu;

monga mwa unyinji wa nsoni zanu zokoma

mufafanize machimo anga.

2 Yes. 1.16; 1Yoh. 1.7, 9 Mubwereze kunditsuka mphulupulu yanga,

ndipo mundiyeretse kundichotsera choipa changa.

3 Mas. 32.5 Chifukwa ndazindikira machimo anga;

ndipo choipa changa chili pamaso panga chikhalire.

4 Gen. 39.9; 2Sam. 12.13; Aro. 3.4 Pa Inu, Inu nokha, ndinachimwa,

ndipo ndinachichita choipacho pamaso panu;

kuti mukhale wolungama pakulankhula Inu,

mukhalenso woyera pa kuweruza kwanu.

5 Yob. 14.4; Aro. 5.12 Onani, ndinabadwa m'mphulupulu,

ndipo mai wanga anandilandira m'zoipa.

6 Yob. 38.36 Onani, Inu mukondwera ndi zoonadi m'malo a m'katimo;

ndipo m'malo a m'tseri mudzandidziwitsa nzeru.

7 Num. 19.18; Yes. 1.18 Mundiyeretse ndi hisope ndipo ndidzayera;

munditsuke ndipo ndidzakhala wa mbuu woposa matalala.

8Mundimvetse chimwemwe ndi kusekera,

kuti mafupawo munawathyola akondwere.

9 Yer. 16.17 Muzibisire nkhope yanu zolakwa zanga,

ndipo mufafanize mphulupulu zanga zonse.

10 Ezk. 11.19; 36.25-26; Aef. 4.23-24 Mundilengere mtima woyera, Mulungu;

mukonze mzimu wokhazikika m'kati mwanga.

11 Aro. 8.9; Aef. 4.30 Musanditaye kundichotsa pamaso panu;

musandichotsere Mzimu wanu Woyera.

12 2Ako. 3.17 Mundibwezere chimwemwe cha chipulumutso chanu;

ndipo mzimu wakulola undigwirizize.

13Pomwepo ndidzalangiza ochimwa njira zanu;

ndipo olakwa adzabwera kwa Inu.

14 2Sam. 11.15, 17; 12.9 Mundilanditse kumlandu wa mwazi, Mulungu,

ndinu Mulungu wa chipulumutso changa;

lilime langa lidzakweza nyimbo ya chilungamo chanu.

15Ambuye, tsegulani pa milomo yanga;

ndipo pakamwa panga padzalalikira ulemekezo wanu.

16 Mas. 50.8 Pakuti simukondwera ndi nsembe, mwenzi nditapereka;

nsembe yopsereza simuikonda.

17 Mas. 34.18; Yes. 57.15 Nsembe za Mulungu ndizo mzimu wosweka;

Inu, Mulungu, simudzaupeputsa mtima wosweka ndi wolapa.

18Chitirani Ziyoni chokoma monga mwa kukondwera kwanu;

mumange malinga a miyala a Yerusalemu.

19 Mala. 3.3 Pamenepo mudzakondwera nazo nsembe zachilungamo,

ndi nsembe yopsereza ndi yopsereza yathunthu;

pamenepo adzapereka

ng'ombe paguwa lanu la nsembe.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help