YONA 2 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

Pemphero la Yona ali m'mimba mwa chinsomba

1Pamenepo Yona anapemphera kwa Yehova Mulungu wake ali m'mimba mwa nsombayo.

2Mas. 120.1Ndipo anati,

Ndinaitana Yehova m'nsautso wanga,

ndipo anandiyankha ine;

ndinafuula ndili m'mimba ya manda,

ndipo munamva mau anga.

3 Mas. 42.7; 88.6 Pakuti munandiponya mwakuya m'kati mwa nyanja,

ndipo madzi anandizinga;

mafunde anu onse a nyondonyondo anandimiza.

4Ndipo ndinati, Ndatayika ndichoke pamaso panu;

koma ndidzapenyanso Kachisi wanu wopatulika.

5 Mas. 69.1 Madzi anandizinga mpaka moyo wanga,

madzi akuya anandizungulira,

kayandeyande wa m'nyanja anandikulunga mutu.

6 Mas. 16.10 Ndinatsikira kumatsinde a mapiri,

mipingiridzo ya dziko inanditsekereza kosatha;

koma munandikwezera moyo wanga

kuuchotsa kuchionongeko, Yehova Mulungu wanga.

7 Mas. 18.6 Pokomoka moyo wanga m'kati mwanga ndinakumbukira Yehova;

ndi pemphero langa linafikira Inu mu Kachisi wanu wopatulika.

8Iwo osamalira mabodza opanda pake

ataya chifundo chaochao.

9 Mas. 3.8; 116.17-18 Koma ine ndidzakupherani Inu nsembe ndi mau akuyamika,

ndidzakwaniritsa chowinda changa.

Chipulumutso ncha Yehova.

10Pamenepo Yehova analankhula ndi nsombayo, ndipo inamsanzira Yona kumtunda.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help