MASALIMO 93 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

Ufumu wa Mulungu ndiwo wa ulemerero, mphamvu, ndi chiyero

1 Mas. 147.1 Yehova achita ufumu; wadziveka ndi ukulu;

wadziveka Yehova, wadzimangirira mphamvu m'chuuno;

dziko lomwe lokhalamo anthu likhakizika, silidzagwedezeka.

2 Mas. 45.6 Mpando wachifumu wanu ukhazikika kuyambira kale lija;

Inu ndinu wosayambira ndi kale lomwe.

3Mitsinje ikweza, Yehova,

mitsinje ikweza mkokomo wao;

mitsinje ikweza mafunde ao.

4 Mas. 65.7; 89.9 Yehova Wam'mwamba ndiye wamphamvu,

wakuposa mkokomo wa madzi ambiri,

ndi mafunde olimba a nyanja.

5Mboni zanu zivomerezeka ndithu;

chiyero chiyenera nyumba yanu,

Yehova, kunthawi za muyaya.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help