1 Mas. 89.1 Ndidzaimba zachifundo ndi chiweruzo;
ndidzaimba zakukulemekezani Inu, Yehova.
2 1Maf. 9.4 Ndidzachita mwanzeru m'njira yangwiro;
mudzandidzera liti?
Ndidzayenda m'nyumba mwanu ndi mtima wangwiro.
3 Mas. 97.10 Sindidzaika chinthu choipa pamaso panga;
chochita iwo akupatuka padera chindiipira;
sichidzandimamatira.
4Mtima wopulukira udzandichokera;
sindidzadziwana naye woipa.
5 Mas. 15.3; Miy. 6.17 Wakuneneza mnzake m'tseri ndidzamdula;
wa maso odzikuza ndi mtima wodzitama sindidzamlola.
6Maso anga ayang'ana okhulupirika m'dziko, kuti akhale ndi Ine;
iye amene ayenda m'njira yangwiro, iyeyu adzanditumikira Ine.
7 Mas. 120.2 Wakuchita chinyengo sadzakhala m'kati mwa nyumba yanga;
wakunena mabodza sadzakhazikika pamaso panga.
8 Yer. 21.12 Mamawa onse ndidzadula oipa onse a m'dziko;
kuduliratu onse akuchita zopanda pake kumzinda wa Yehova.
Who We AreWhat We EelieveWhat We Do
2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.