MASALIMO 113 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

Anthu onse alemekeze dzina la Mulungu wothandiza aumphawi

1 Mas. 135.1 Aleluya;

Lemekezani, inu atumiki a Yehova;

lemekezani dzina la Yehova.

2Lodala dzina la Yehova Kuyambira tsopano kufikira kosatha.

3 Yes. 59.19 Chitulukire dzuwa kufikira kulowa kwake

lilemekezedwe dzina la Yehova.

4Yehova akwezeka pamwamba pa amitundu onse,

ulemerero wake pamwambamwamba.

5 Mas. 89.6 Akunga Yehova Mulungu wathu ndani?

Amene akhala pamwamba patali,

6 Yes. 57.15 nadzichepetsa apenye

zam'mwamba ndi za padziko lapansi.

7 1Sam. 2.8 Amene autsa wosauka kumchotsa kufumbi,

nakweza waumphawi kumchotsa kudzala.

8Kuti amkhalitse pamodzi ndi akulu,

pamodzi ndi akulu a anthu ake.

9 1Sam. 2.5; Yes. 54.1; Agal. 4.27 Asungitsa nyumba mkazi wosaona mwana,

akhale mai wokondwera ndi ana.

Aleluya.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help