MASALIMO 120 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

Apempha Mulungu amlanditse pa omnamizaNyimbo yokwerera.

1 Mas. 118.5; Yon. 2.2 Ndinafuulira kwa Yehova mu msauko wanga,

ndipo anandivomereza.

2Yehova, landitsani moyo wanga kumilomo ya mabodza,

ndi kulilime lonyenga.

3Adzakuninkhanji, adzakuonjezeranji,

lilime lonyenga iwe?

4Mivi yakuthwa ya chiphona,

ndi makala tsanya.

5 Gen. 25.13; Ezk. 27.13 Tsoka ine, kuti ndili mlendo mu Meseki,

kuti ndigonera m'mahema a Kedara!

6Moyo wanga unakhalitsa nthawi

pamodzi ndi iye wakudana nao mtendere.

7Ine ndikuti, Mtendere;

koma polankhula ine, iwowa akuti, Nkhondo.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help