MASALIMO 141 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

Davide apempha Mulungu amthandize poyesedwa ndi zoipaSalimo la Davide.

1 Mas. 70.5 Yehova, ndaitana kwa Inu; ndifulumireni ine;

munditcherere khutu, pamene ndiitana kwa Inu.

2 Chiv. 8.3-4 Pemphero langa liikike ngati chofukiza pamaso panu;

kukweza manja anga kuikike ngati nsembe ya madzulo.

3Muike mdindo pakamwa panga, Yehova;

sungani pakhomo pa milomo yanga.

4 Miy. 23.6 Mtima wanga usalinge kuchinthu choipa,

kuchita ntchito zoipa

ndi anthu akuchita zopanda pake;

ndipo ndisadye zankhuli zao.

5 Miy. 9.8; 19.25; 25.12 Akandipanda munthu wolungama ndidzati nchifundo:

akandidzudzula, ndidzakuyesa mafuta a pamutu;

mutu wanga usakane:

Pakuti pangakhale posautsidwa iwo ndidzawapempherera.

6Oweruza ao anagwetseka pambali pa thanthwe;

nadzamva mau anga kuti ndiwo okondweretsa.

7Mafupa athu amwazika pakamwa pa manda,

monga ngati akumba nanyimphula nthaka yapansi.

8 2Mbi. 20.12 Pakuti maso anga apenya kwanu, Yehova Ambuye;

ndithawira kwa Inu; musataye moyo wanga.

9 Mas. 119.110 Mundisunge ndisagwe mumsampha ananditcherawo,

ndisakodwe m'makwekwe a iwo ochita zopanda pake.

10 Mas. 35.8 Oipa agwe pamodzi m'maukonde ao,

kufikira nditapitirira ine.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help