MASALIMO 140 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

Davide apempha Mulungu amlanditse kwa mdani woipa wamphamvuKwa Mkulu wa Nyimbo: Salimo la Davide.

1Ndilanditseni, Yehova, kwa munthu woipa;

ndisungeni kwa munthu wachiwawa;

2amene adzipanga zoipa mumtima mwao;

masiku onse amemeza nkhondo.

3 Aro. 3.13 Anola lilime lao ngati njoka;

pansi pa milomo yao pali ululu wa mphiri.

4 Mas. 71.4 Ndilindireni Yehova, ndisalowe m'manja mwa woipa;

ndisungeni kwa munthu wachiwawa;

kwa iwo akuti akankhe mapazi anga.

5 Yer. 18.22 Odzikuza ananditchera msampha, nandibisira zingwe;

anatcha ukonde m'mphepete mwa njira;

ananditchera makwekwe.

6Ndinati kwa Yehova, Inu ndinu Mulungu wanga;

munditcherere khutu mau a kupemba kwanga, Yehova.

7Yehova Ambuye, ndinu mphamvu ya chipulumutso changa,

munandiphimba mutu wanga tsiku lakulimbana nkhondo.

8Yehova, musampatse woipa zokhumba iye;

musamthandize zodzipanga zake; angadzikuze.

9 Miy. 18.7 Kunena za mutu wao wa iwo akundizinga,

choipa cha milomo yao chiwaphimbe.

10Makala amoto awagwere;

aponyedwe kumoto;

m'maenje ozama, kuti asaukenso.

11Munthu wamlomo sadzakhazikika padziko lapansi;

choipa chidzamsaka munthu wachiwawa kuti chimgwetse.

12 1Maf. 8.45 Ndidziwa kuti Yehova adzanenera wozunzika mlandu,

ndi kuweruzira aumphawi.

13 Mas. 11.7 Indedi, olungama adzayamika dzina lanu;

oongoka mtima adzakhala pamaso panu.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help