MASALIMO 3 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

Kukhulupirika kwa MulunguSalimo la Davide, muja anathawa Abisalomu mwana wake.

1 2Sam. 15.18 Yehova! Ha! Achuluka nanga akundisautsa ine!

Akundiukira ine ndi ambiri.

2 Mas. 71.11 Ambiri amati kwa moyo wanga,

alibe chipulumutso mwa Mulungu.

3 Gen. 15.1; Mas. 28.7 Ndipo Inu Yehova, ndinu chikopa changa;

ulemerero wanga, ndi wondiweramutsa mutu wanga.

4 Mas. 34.4 Ndifuula kwa Yehova ndi mau anga,

ndipo andiyankha m'phiri lake loyera.

5 Mas. 4.8 Ndinagona ine pansi, ndinagona tulo;

ndinauka; pakuti Yehova anandichirikiza.

6 Mas. 27.3 Sindidzaopa unyinji wa anthu akundizinga ine.

7 Mas. 7.6 Ukani Yehova; ndipulumutseni, Mulungu wanga!

Pakuti mwapanda adani anga onse patsaya;

mwawathyola mano oipawo.

8 Yes. 43.11 Chipulumutso ncha Yehova;

dalitso lanu likhale pa anthu anu.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help