MASALIMO 129 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

Israele asautsidwa koma osafafanizidwaNyimbo yokwerera.

1Anandisautsa kawirikawiri kuyambira ubwana wanga,

anene tsono Israele;

2 Yoh. 16.33 Anandisautsa kawirikawiri kuyambira ubwana wanga;

koma sanandilake.

3Olima analima pamsana panga;

anatalikitsa mipere yao.

4Yehova ndiye wolungama;

anadulatu zingwe za oipa.

5Achite manyazi nabwerere m'mbuyo.

Onse akudana naye Ziyoni.

6 Mas. 37.2 Akhale ngati udzu womera patsindwi,

wakufota asanauzule;

7umene womweta sadzaza nao dzanja lake,

kapena womanga mitolo sakupatira manja.

8 Rut. 2.4; Mas. 118.26; Yes. 8.18 Angakhale opitirirapo sanena,

Dalitso la Mulungu likhale pa inu;

tikudalitsani m'dzina la Yehova.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help