1 Mas. 29.9 Kodi udziwa nyengo yakuswana zinkhoma?
Kodi wapenyerera pakuswa mbawala?
2Ukhoza kodi kuwerenga miyezi yakuzipitira,
kapena udziwa nyengo yoti ziswane?
3Zithuntha, ziswa,
zitaya zowawa zao.
4Ana ao akhala ojincha, akulira kuthengo,
achoka osabwerera kwa amao.
5Ndani walola mbidzi ituluke yaufulu?
Anaimasulira mbidzi nsinga zake ndani,
6 Yer. 2.24 imene ndachiyesa chipululu nyumba yake,
ndi dziko lakhulo pokhala pake?
7Aseka phokoso la kumzinda,
osamva kukuwa kwa wofulumiza nyama za m'goli.
8Poyenda ponse pamapiri mpa busa pake;
ilondola chachiwisi chilichonse.
9Kodi njati idzavomera kukutumikira,
idzakhala ku chodyetseramo chako kodi?
10Kodi ukhoza kumanga njati ndi lamba lake ilime m'mchera?
Kapena idzakutsata kodi kufafaniza nthumbira m'zigwa?
11Udzaikhulupirira kodi, popeza mphamvu yake njaikulu?
Udzaisiyira ntchito yako kodi?
12Kodi udzaitama kuti itute mbeu zako,
ndi kuzisonkhanitsira kudwale?
13Phiko la nthiwatiwa likondwera,
koma mapiko ndi nthenga zake nzofatsa kodi?
14Pakuti isiya mazira ake panthaka,
nimafunditsa m'fumbi,
15nkuiwala kuti phazi lingawaphwanye,
kapena chilombo chingawapondereze.
16Iumira mtima ana ake monga ngati sali ake;
idzilemetsa ndi ntchito chabe, popeza ilibe mantha;
17pakuti Mulungu anaimana nzeru,
ndipo sanaigawire luntha.
18Ikafika nthawi yake, iweramuka,
iseka kavalo ndi wa pamsana pake.
19Wampatsa kavalo mphamvu yake kodi?
Wamveka pakhosi pake chenjerere chogwedezeka?
20Wamlumphitsa kodi ngati dzombe?
Ulemerero wa kumina kwake ngwoopsa.
21 Yer. 8.6 Apalasa kuchigwa, nakondwera nayo mphamvu yake;
atuluka kukomana nao eni zida.
22Aseka mantha osaopsedwa,
osabwerera kuthawa lupanga.
23Phodo likuti kochokocho panthiti pake,
mkondo wonyezimira ndi nthungo yomwe.
24Ndi kunjenjemera kwaukali aimeza nthaka,
osaimitsika pomveka lipenga.
25Pomveka lipenga akuti, Hee!
Anunkhiza nkhondo ilikudza kutali,
kugunda kwa akazembe ndi kuhahaza.
26Kodi kabawi auluka mwa nzeru zako,
natambasula mapiko ake kunka kumwera?
27 Yer. 49.16 Kodi chiombankhanga chikwera m'mwamba pochilamulira iwe,
nkumanga chisanja chake m'mwamba?
28Kwao nkuthanthwe, chigona komweko,
pansonga pa thanthwe pokhazikikapo.
29Pokhala kumeneko chiyang'ana chakudya;
maso ake achipenyetsetsa chili kutali.
30 Mat. 24.28 Ana ake akumwa mwazi,
ndipo pomwe pali ophedwa, apo pali icho.
Who We AreWhat We EelieveWhat We Do
2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.