MASALIMO 115 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

Mulungu ndi wa ulemerero, mafano ndiwo achabe

1 Yes. 48.11 Kwa ife ai, Yehova, kwa ife ai,

koma kwa dzina lanu patsani ulemerero,

chifukwa cha chifundo chanu, ndi choonadi chanu.

2 Mas. 42.3; Yow. 2.17 Aneneranji amitundu,

Ali kuti Mulungu wao?

3 1Mbi. 16.26 Koma Mulungu wathu ndiye ali m'mwamba;

achita chilichonse chimkonda.

4 Mas. 135.15-18 Mafano ao ndiwo a siliva ndi golide,

ntchito za manja a anthu.

5Pakamwa ali napo, koma osalankhula;

maso ali nao, koma osapenya;

6makutu ali nao, koma osamva;

mphuno ali nazo, koma osanunkhiza;

7manja ali nao, koma osagwira;

mapazi ali nao, koma osayenda;

kapena sanena pammero pao.

8 Hab. 2.18-19 Adzafanana nao iwo akuwapanga;

ndi onse akuwakhulupirira.

9 Mas. 62.8 Israele, khulupirira Yehova:

Ndiye mthandizi wao ndi chikopa chao.

10 Mas. 118.3 Nyumba ya Aroni, khulupirira Yehova:

Ndiye mthandizi wao, ndi chikopa chao.

11Inu akuopa Yehova, khulupirirani Yehova;

ndiye mthandizi wao ndi chikopa chao.

12Yehova watikumbukira; adzatidalitsa:

adzadalitsa nyumba ya Israele;

adzadalitsa nyumba ya Aroni.

13 Mas. 128.1-4 Adzadalitsa iwo akuopa Yehova,

aang'ono ndi aakulu.

14Yehova akuonjezereni dalitso,

inu ndi ana anu.

15Odalitsika inu a kwa Yehova,

wakulenga kumwamba ndi dziko lapansi.

16Kunena za kumwamba, kumwamba ndiko kwa Yehova;

koma dziko lapansi analipereka kwa ana a anthu.

17 Yes. 38.18 Akufa salemekeza Yehova,

kapena aliyense wakutsikira kuli chete:

18 Dan. 2.20 Koma ife tidzalemekeza Yehova

kuyambira tsopano kufikira nthawi yonse.

Aleluya.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help