MLALIKI 1 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

Za pansi pano nzachabe

1 Mlal. 1.12 Mau a Mlaliki, mwana wa Davide, mfumu ya mu Yerusalemu.

2Mas. 39.5-6; Mlal. 12.8; Aro. 8.20Zachabechabe, ati Mlaliki; zachabechabe zonse ndi chabe.

3Kodi ntchito zake zonse munthu asauka nazo zimpindulira chiyani?

4Mas. 90.5Mbadwo wina upita, mbadwo wina nufika; koma dziko lingokhalabe masiku onse.

5Mas. 19.5-6Inde dzuwa lituluka, nililowa, nilifulumira komwe linatulukako.

6Yoh. 3.8Kulowa kumwera ndi kuzungulira kumpoto zungulirezungulire imaomba mphepo; ibweranso monga mwa mazunguliridwe ake.

7Mitsinje yonse ithira m'nyanja, koma nyanja yosadzala; komwe imukira mitsinjeyo, komweko ibweranso.

8Miy. 27.20Zinthu zonse zilemetsa; munthu sangathe kuzifotokoza; maso sakhuta m'kuona, ndi makutu sakhuta m'kumva.

9Chomwe chinaoneka chidzaonekanso; ndi chomwe chinachitidwa chidzachitidwanso; ndipo palibe kanthu katsopano pansi pano.

10Kodi pali kanthu unganene kuti, Taona katsopano aka? Kanalipo kale, kale lomwe tisanabadwe ife.

11Zoyamba zija sizikumbukiridwa; ngakhale zomwe zilinkudzazo, omwe adzakhalabe m'tsogolomo, sadzazikumbukirai.

12Ine Mlaliki ndinali mfumu ya Israele mu Yerusalemu.

13Gen. 3.19Ndipo ndinapereka mtima kufunafuna ndi nzeru, ndi kulondetsa zonse zimachitidwa pansi pa thambo; ntchito yovuta imeneyi Mulungu apatsa ana a anthu akasauke nayo.

14Ndaona ntchito zonse zipangidwa kunja kuno; ndipo zonsezo ndi chabe ndi kungosautsa mtima.

15Chokhotakhota sichingaongokenso; ndipo choperewera sichingawerengedwe.

161Maf. 3.12-13Ndinalankhula ndi mtima wanga, ndi kuti, Taona, ndakuza ndi kudzienjezera nzeru koposa onse anakhala mu Yerusalemu ndisanabadwe ine; inde mtima wanga wapenyera kwambiri nzeru ndi chidziwitso.

171Ate. 5.21Ndipo ndinapereka mtima kudziwa nzeru ndi kudziwa misala ndi utsiru; ndinazindikira kuti ichinso chingosautsa mtima.

18Pakuti m'nzeru yambiri muli chisoni chambiri; ndi yemwe aenjezera chidziwitso aenjezera zowawa.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help