YOBU 25 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

Bilidadi akuti munthu sayenera kudziyesa wolungama pamaso pa Mulungu

1Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha, nati,

2Kulamulira ndi kuopsa kuli ndi Iye;

achita mtendere pa zam'mwamba zake.

3 Yak. 1.17 Ngati awerengedwa makamu ake?

Ndipo ndaniyo, kuunika kwake sikumtulukira?

4 Mas. 130.3-4 Potero munthu akhala bwanji wolungama kwa Mulungu?

Kapena wobadwa ndi mkazi akhala woyera bwanji?

5Taonani, ngakhale mwezi ulibe kuwala;

ndi nyenyezi siziyera pamaso pake;

6 Mas. 22.6 kopambana kotani nanga munthu, ndiye mphutsi!

Ndi wobadwa ndi munthu, ndiye nyongolotsi!

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help