1 Mas. 128.1; 119.16, 47 Aleluya.
Wodala munthu wakuopa Yehova,
wakukondwera kwambiri ndi malamulo ake.
2 Mas. 25.13 Mbeu yake idzakhala yamphamvu padziko lapansi;
mbadwo wa oongoka mtima udzadalitsidwa.
3 Mat. 6.33 M'nyumba mwake mudzakhala akatundu ndi chuma:
Ndi chilungamo chake chikhala chikhalire.
4 Mas. 97.11 Kuunika kutulukira oongoka mtima mumdima;
Iye ndiye wachisomo, ndi wansoni ndi wolungama.
5 Luk. 6.35 Wodala munthu wakuchitira chifundo, nakongoletsa;
adzalimbika nao mlandu wake poweruzidwa.
6 Miy. 10.7 Popeza sadzagwedezeka nthawi zonse;
wolungama adzakumbukika ku nthawi yosatha.
7 Miy. 1.33 Sadzaopa mbiri yoipa;
mtima wake ngwokhazikika, wokhulupirira Yehova.
8Mtima wake ngwochirikizika, sadzachita mantha,
kufikira ataona chofuna iye pa iwo omsautsa.
9 2Ako. 9.9 Anagawagawa, anapatsa aumphawi;
chilungamo chake chikhalitsa kosatha;
nyanga yake idzakwezeka ndi ulemu.
10 Miy. 10.28; Luk. 13.28 Woipa adzaziona, nadzapsa mtima;
adzakukuta mano, nadzasungunuka;
chokhumba oipa chidzatayika.
Who We AreWhat We EelieveWhat We Do
2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.