MASALIMO 148 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

Zolengedwa zonse zilemekeze Mulungu

1 Aleluya.

Lemekezani Yehova kochokera kumwamba;

mlemekezeni m'misanje.

2Mlemekezeni, angelo ake onse;

mlemekezeni, makamu ake onse.

3Mlemekezeni, dzuwa ndi mwezi;

mlemekezeni, nyenyezi zonse zounikira.

4 1Maf. 8.27 Mlemekezeni, m'mwambamwamba,

ndi madzi inu, a pamwamba pa thambo.

5Alemekeze dzina la Yehova;

popeza analamulira, ndipo zinalengedwa.

6 Yer. 31.35-36 Anazikhazikanso kunthawi za nthawi;

anazipatsa chilamulo chosatumphika.

7Lemekezani Yehova kochokera ku dziko lapansi,

zinsomba inu, ndi malo ozama onse;

8moto ndi matalala, chipale chofewa ndi nkhungu;

mphepo ya namondwe, yakuchita mau ake;

9 Yes. 55.12 mapiri ndi zitunda zonse;

mitengo yazipatso ndi yamikungudza yonse:

10Nyama zakuthengo ndi zoweta zonse;

zokwawa, ndi mbalame zakuuluka.

11Mafumu a padziko ndi mitundu yonse ya anthu;

zinduna ndi oweruza onse a padziko.

12Anyamata ndiponso anamwali;

okalamba pamodzi ndi ana.

13 Yes. 12.4 Alemekeze dzina la Yehova;

pakuti dzina lake lokha ndi lokwezeka;

ulemerero wake uli pamwamba padziko lapansi ndi thambo.

14 Aef. 2.17 Ndipo anakweza nyanga ya anthu ake,

chilemekezo cha okondedwa ake onse;

ndiwo ana a Israele, anthu a pafupi pa Iye.

Aleluya.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help