MIYAMBO 15 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

1 Ower. 8.1-3; 1Sam. 25.10-13 Mayankhidwe ofatsa abweza mkwiyo;

koma mau owawitsa aputa msunamo.

2Lilime la anzeru linena bwino zomwe adziwa;

koma m'kamwa mwa opusa mutsanulira utsiru.

3 Yer. 16.17; Aheb. 4.13 Maso a Yehova ali ponseponse,

nayang'anira oipa ndi abwino.

4Kuchiza lilime ndiko mtengo wa moyo;

koma likakhota liswa moyo.

5Chitsiru chipeputsa mwambo wa atate wake;

koma wosamalira chidzudzulo amachenjera.

6M'nyumba ya wolungama muli katundu wambiri;

koma m'phindu la woipa muli vuto.

7Milomo ya anzeru iwanditsa nzeru,

koma mtima wa opusa suli wolungama.

8 Yes. 1.11; Yer. 6.20 Nsembe ya oipa inyansa Yehova;

koma pemphero la oongoka mtima limkondweretsa.

9 1Tim. 6.11 Njira ya oipa inyansa Yehova;

koma akonda wolondola chilungamo.

10 1Maf. 22.8 Wosiya njira adzalangidwa mowawa;

wakuda chidzudzulo adzafa.

11 2Mbi. 6.30; Yoh. 2.24-25 Kumanda ndi kuchionongeko kuli pamaso pa Yehova;

koposa kotani nanga mitima ya ana a anthu?

12 2Tim. 4.3 Wonyoza sakonda kudzudzulidwa,

samapita kwa anzeru.

13 Miy. 17.22 Mtima wokondwa usekeretsa nkhope;

koma moyo umasweka ndi zowawa za m'mtima.

14Mtima wa wozindikira ufunitsa kudziwa;

koma m'kamwa mwa opusa mudya utsiru.

15Masiku onse a wosauka ali oipa;

koma wokondwera mtima ali ndi phwando losatha.

16 Mas. 37.16; 1Tim. 6.6 Zapang'ono, ulikuopa Yehova,

zipambana ndi katundu wambiri pokhala phokoso.

17 Miy. 17.1 Kudya masamba, pali chikondano,

kuposa ng'ombe yonenepa pali udani.

18Munthu wozaza aputa makani;

koma wosakwiya msanga atonthoza makangano.

19Mayendedwe a waulesi akunga linga laminga,

koma njira ya oongoka mtima iundidwa ngati mseu.

20Mwana wanzeru akondweretsa atate wake;

koma munthu wopusa apeputsa amake.

21 Aef. 5.15 Wosowa nzeru akondwera ndi utsiru;

koma munthu wozindikira aongola mayendedwe ake.

22Zolingalira zizimidwa popanda upo;

koma pochuluka aphungu zikhazikika.

23Munthu akondwera ndi mayankhidwe a m'kamwa mwake;

ndi mau a pa nthawi yake kodi sali abwino?

24 Afi. 3.20 Anzeru ayesa njira yamoyo yokwerakwera,

kuti apatuke kusiya kunsi kwa manda.

25 Mas. 68.5-6 Yehova adzapasula nyumba ya wonyada;

koma adzalembera mkazi wamasiye malire ake.

26Ziwembu zoipa zinyansa Yehova;

koma oyera mtima alankhula mau okondweretsa.

27 Yes. 5.8 Wopindula monyenga avuta nyumba yake;

koma wakuda mitulo adzakhala ndi moyo.

28 1Pet. 3.15 Mtima wa wolungama uganizira za mayankhidwe;

koma m'kamwa mwa ochimwa mutsanulira zoipa.

29 Mas. 34.16; 145.18-19 Yehova atalikira oipa;

koma pemphero la olungama alimvera.

30Kuunika kwa maso kukondweretsa mtima;

ndipo pomveka zabwino mafupa amatenga uwisi.

31Khutu lomvera chidzudzulo cha moyo

lidzakhalabe mwa anzeru.

32Wokana mwambo apeputsa moyo wake;

koma wosamalira chidzudzulo amatenga nzeru.

33 Miy. 1.7 Kuopa Yehova ndiko mwambo wanzeru;

ndipo chifatso chitsogolera ulemu.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help