1 Deut. 25.13-16 Muyeso wonyenga unyansa Yehova;
koma mulingo wamphumphu umsekeretsa.
2 Dan. 4.30-31 Pakudza kudzikuza padzanso manyazi;
koma nzeru ili ndi odzichepetsa.
3Kuongoka mtima kwa olungama kuwatsogolera;
koma kukhota kwa achiwembu kudzawaononga.
4 Gen. 7.1; Ezk. 7.19 Chuma sichithandiza tsiku la mkwiyo;
koma chilungamo chipulumutsa kuimfa.
5Chilungamo cha wangwiro chimaongola njira yake;
koma woipa adzagwa ndi zoipa zake.
6 Mlal. 10.8 Chilungamo cha oongoka mtima chidzawapulumutsa;
koma achiwembu adzagwidwa ndi mphulupulu yao.
7Pomwalira woipa chidikiro chake chionongeka;
chiyembekezo cha uchimo chionongeka.
8Wolungama apulumuka kuvuto;
woipa nalowa m'malo mwake.
9 Yob. 8.13 Wonyoza Mulungu aononga mnzake ndi m'kamwa mwake;
koma olungama adzapulumuka pakudziwa.
10Olungama akapeza bwino, mzinda usekera;
nufuula pakuonongeka oipa.
11Madalitso a olungama akuza mzinda;
koma m'kamwa mwa oipa muupasula.
12 Lev. 19.16 Wopeputsa mnzake asowa nzeru;
koma wozindikira amatonthola.
13Kazitape woyendayenda amawanditsa zinsinsi;
koma wokhulupirika mtima abisa mau.
14 1Maf. 12.1-19 Popanda upo wanzeru anthu amagwa;
koma pochuluka aphungu pali chipulumutso.
15Woperekera mlendo chikole adzaphwetekwapo;
koma wakuda chikole akhala ndi mtendere.
16 Miy. 31.30 Mkazi wodekha agwiritsa ulemu;
aukali nagwiritsa chuma.
17 Mat. 5.7 Wachifundo achitira moyo wake zokoma;
koma wankhanza avuta nyama yake.
18 Hos. 10.12 Woipa alandira malipiro onyenga;
koma wofesa chilungamo aonadi mphotho.
19Wolimbikira chilungamo alandira moyo;
koma wolondola zoipa adzipha yekha.
20Okhota mtima anyansa Yehova;
koma angwiro m'njira zao amsekeretsa.
21 Mas. 112.2 Zoonadi, wochimwa sadzapulumuka chilango;
koma mbeu ya olungama idzalanditsidwa.
22Monga chipini chagolide m'mphuno ya nkhumba,
momwemo mkazi wokongola wosasinkhasinkha bwino.
23Chifuniro cha olungama chifikitsa zabwino zokha;
koma chiyembekezo cha oipa mkwiyo.
24 Mas. 112.9 Alipo wogawira, nangolemerabe;
aliponso womana chomwe ayenera kupatsa nangosauka.
25 2Ako. 9.6-9 Mtima wa mataya udzalemera;
wothirira madzi nayenso adzathiriridwa.
26 Amo. 8.4-6 Womana tirigu anthu amtemberera;
koma madalitso adzakhala pamutu pa wogulitsa.
27Wopwaira ubwino afunitsa chikondwerero;
koma zoipa zidzamfikira wozilondola.
28 Yer. 17.8; Mrk. 10.24 Wokhulupirira chuma chake adzagwa;
koma olungama adzaphuka ngati tsamba.
29Wovuta banja lake adzalowa m'zomsautsa;
wopusa adzatumikira wanzeru.
30 Dan. 12.3; 1Ako. 9.19-23; Yak. 5.20 Chipatso cha wolungama ndi mtengo wa moyo;
ndipo wokola mtima ali wanzeru.
31 Yer. 25.29; 1Pet. 4.17-18 Taonani, wolungama adzalandira mphotho kunja kuno;
koposa kotani woipa ndi wochimwa?
Who We AreWhat We EelieveWhat We Do
2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.