MASALIMO 12 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

Anthu ndi amabodza, Mulungu ndiye woonaKwa Mkulu wa Nyimbo: pa Seminiti. Salimo la Davide.

1 Yes. 57.1 Pulumutsani, Yehova; pakuti wofatsa wasowa;

pakuti okhulupirika achepa mwa ana a anthu.

2 Mas. 144.8; Yer. 9.8 Amanena za bodza munthu yense ndi mnansi wake,

amanena ndi mlomo wothyasika, ndi mitima iwiri.

3 Mas. 144.8; Yer. 9.8 Yehova adzadula milomo yonse yothyasika,

lilime lakudzitamandira;

4amene amati, Ndi lilime lathu tidzaposa;

milomo yathu nja ife eni; mbuye wa pa ife ndani?

5 Eks. 3.7-8 Chifukwa cha kupasuka kwa ozunzika,

chifukwa cha kuusa moyo kwa aumphawi,

ndiuka tsopano, ati Yehova;

ndidzamlonga mosungika muja alakalakamo.

6 Mas. 19.8-9 Mau a Yehova ndi mau oona;

ngati siliva woyenga m'ng'anjo yadothi,

yoiyeretsa kasanu ndi kawiri.

7Mudzawasunga, Yehova,

mudzawatchinjirizira mbadwo uno kunthawi zonse.

8Oipa amayenda mozungulirazungulira,

potamanda iwo chonyansa mwa ana a anthu.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help