MASALIMO 125 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

Okhulupirira Yehova akhazikika mtimaNyimbo yokwerera.

1Iwo akukhulupirira Yehova

akunga phiri la Ziyoni, losasunthika, likhazikika kosatha.

2Monga mapiri azinga Yerusalemu,

momwemo Yehova azinga anthu ake,

kuyambira tsopano kufikira nthawi zonse.

3 Yes. 14.5 Pakuti ndodo yachifumu ya choipa siidzapumula pa gawo la olungama;

kuti olungama asatulutse dzanja lao kuchita chosalungama.

4Chitirani chokoma, Yehova, iwo okhala okoma;

iwo okhala oongoka mumtima mwao.

5 Miy. 2.15; Agal. 6.16 Koma iwo akupatula kutsata njira zao zokhotakhota,

Yehova adzawachotsa pamodzi ndi ochita zopanda pake.

Mtendere ukhale pa Israele.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help