MLALIKI 7 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

Kumva zowawa nkokoma, nzeru ndi kudziletsa momwemo

1 Miy. 22.1 Mbiri yabwino iposa zonunkhira zabwino; ndi tsiku lakumwalira liposa tsiku lakubadwa.

2Kunka kunyumba ya maliro kupambana kunka kunyumba ya madyerero; pakuti kujako ndi matsiriziro a anthu onse; ndipo omwe ali ndi moyo adzakumbukirapo.

32Ako. 7.10Chisoni chiposa kuseka; pakuti nkhope yakugwa ikonza mtima.

4Mtima wa anzeru uli m'nyumba ya maliro; koma mtima wa zitsiru uli m'nyumba ya kuseka.

5Mas. 141.5Kumva chidzudzulo cha anzeru kupambana kumva nyimbo ya zitsiru.

6Pakuti kuseka kwa chitsiru kunga minga ilikuthetheka pansi pa mphika; ichinso ndi chabe.

7Deut. 16.19Indetu nsautso uyalutsa wanzeru; ndi mtulo uipitsa mtima.

8Miy. 14.29Chitsiriziro cha kanthu chiposa chiyambi chake; wofatsa mtima apambana wodzikuza mtima.

9Miy. 16.32; Yak. 1.19Usakangaze mumtima mwako kukwiya; pakuti mkwiyo ugona m'chifuwa cha zitsiru.

10Usanene, Kodi bwanji masiku akale anapambana ano? Pakuti sulikufunsa mwanzeru pamenepo.

11Nzeru ili yabwino pamodzi ndi cholowa; akuona dzuwa apindula nayo.

12Pakuti nzeru itchinjiriza monga ndalama zitchinjiriza; koma kudziwa kupambana, chifukwa nzeru isunga moyo wa eni ake.

13Yes. 14.27Tapenya ntchito ya Mulungu; pakuti ndani akhoza kulungamitsa chomwe iye anachikhotetsa?

14Deut. 28.45-47Tsiku la mwai kondwera, koma tsiku la tsoka lingirira; Mulungu waika ichi pambali pa chinzake, kuti anthu asapeze kanthu ka m'tsogolo mwao.

15Ndaona zonsezi masiku anga achabe; pali wolungama angofa m'chilungamo chake, ndipo pali woipa angokhalabe ndi moyo m'kuipa kwake.

16Aro. 12.3Usapambanitse kukhala wolungama; usakhale wanzeru koposa; bwanji ufuna kudziononga wekha?

17Mas. 55.23Usapambanitse kuipa, ngakhale kupusa; uferenji nthawi yako isanafike?

18Kuli kwabwino kugwira ichi; indetu, usachotsepo dzanja lako pakuti yemwe aopa Mulungu adzatuluka monsemo.

19Nzeru ilimbitsa wanzeru koposa akulu khumi akulamulira m'mzinda.

201Maf. 8.46; Aro. 3.23; 1Yoh. 1Pakuti kulibe wolungama pansi pano amene achita zabwino osachimwa.

21Mau onsetu onenedwa usawalabadire; kuti usamve kapolo wako alikukutemberera;

22pakuti kawirikawiritu mtima wako udziwa kuti nawenso unatemberera ena.

23 Aro. 1.22 Ndayesa zonsezi ndi nzeru; ndinati, Ndidzakhala wanzeru; koma inanditalikira.

24Chakutali ndi chakuyadi, adzachipeza ndani?

25Ndinapotoka ndi mtima wanga womwe kudziwa ndi kusanthula ndi kufunafuna nzeru ndi malongosoledwe a zinthu, ndi kudziwa kuti udyo ndiwo utsiru, ndi kuti kupusa ndi misala;

26Miy. 5.3-4ndipo ndinapeza kanthu kowawa koposa imfa, ndiko mkazi amene ndiye msampha, mtima wake ukunga maukonde, manja ake ndiwo matangadza; yemwe Mulungu amuyesa wabwino adzapulumuka kwa iye; koma wochimwa adzagwidwa naye.

27Taonani, ichi ndachipeza, ati Mlalikiyo, m'kuphatikiza chinthu china ndi chinzake, ndikazindikire malongosoledwe ao;

28chomwe moyo wanga uchifuna chifunire, koma osachipezai ndi ichi, mwamuna mmodzi mwa chikwi ndinampezadi, koma mkazitu mwa onsewo sindinampeze.

29Gen. 1.27; 3.6-7Taonani, ichi chokha ndachipeza kuti Mulungu analenga anthu oongoka mtima; koma iwowo afunafuna malongosoledwe a mitundumitundu.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help