MASALIMO 6 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

Davide apempha chifundo kwa MulunguKwa Mkulu wa Nyimbo: pa Neginoto, pa Seminiti. Salimo la Davide.

1 Yer. 10.24 Yehova, musandidzudzule mu mkwiyo wanu,

ndipo musandilange muukali wanu.

2 Mas. 41.4 Mundichitire chifundo, Yehova; pakuti ndalefuka ine.

Mundichize, Yehova; pakuti anthunthumira mafupa anga.

3 Yoh. 12.27 Moyo wanganso wanthunthumira kwakukulu;

ndipo Inu, Yehova, kufikira liti?

4Bwererani Yehova, landitsani moyo wanga;

ndipulumutseni chifukwa cha kukoma mtima kwanu.

5 Mas. 30.9 Pakuti muimfa m'mosakumbukira Inu;

m'mandamo adzakuyamikani ndani?

6Ndalema nako kuusa moyo kwanga;

ndiyandamitsa kama wanga usiku wonse;

mphasa yanga ndiolobza ndi misozi yanga.

7 Yob. 17.7 Lapuwala diso langa chifukwa cha chisoni;

lakalamba chifukwa cha onse akundisautsa.

8 Mat. 7.23; 25.41 Chokani kwa ine, nonsenu akuchita zopanda pake;

pakuti wamva Yehova mau a kulira kwanga.

9Wamva Yehova kupemba kwanga;

Yehova adzalandira pemphero langa.

10Adzachita manyazi, nadzanthunthumira kwakukulu

adani anga onse;

adzabwerera, nadzachita manyazi modzidzimuka.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help