MASALIMO 75 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

Mulungu woweruza asiyanitsa pakati pa odzikuza ndi olungamaKwa Mkulu wa Nyimbo: Altasyeti. Salimo la Asafu. Nyimbo.

1Tikuyamikani Inu, Mulungu;

tiyamika, pakuti dzina lanu lili pafupi;

afotokozera zodabwitsa zanu.

2Pakuona nyengo yake ndidzaweruza molunjika.

3Lasungunuka dziko lapansi, ndi onse okhalamo;

ndinachirika mizati yake.

4Ndinati kwa odzitamandira,

musamachita zodzitamandira;

ndi kwa oipa, Musamakweza nyanga;

5musamakwezetsa nyanga yanu;

musamalankhula ndi khosi louma.

6Pakuti kukuzaku sikuchokera kum'mawa,

kapena kumadzulo, kapena kuchipululu.

7 Mas. 50.6; 1Sam. 2.7 Pakuti Mulungu ndiye woweruza;

achepsa wina, nakuza wina.

8 Mas. 60.3 Pakuti m'dzanja la Yehova muli chikho;

ndi vinyo wake achita thovu;

chidzala ndi zosakanizira, ndipo atsanulako.

Indedi, oipa onse a padziko lapansi adzamwa

nadzagugudiza nsenga zake.

9Koma ine ndidzalalikira kosalekeza,

ndidzaimbira zomlemekeza Mulungu wa Yakobo.

10 Mas. 89.17; Yer. 48.25 Ndipo ndidzatseteka nyanga zonse za oipa;

koma nyanga za wolungama zidzakwezeka.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help