MIYAMBO 10 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

Miyambo yosiyanasiyanaMiyambo ya Solomoni:

1 Miy. 29.3, 15 Mwana wanzeru akondweretsa atate;

koma mwana wopusa amvetsa amake chisoni.

2 Dan. 4.27; Luk. 12.19 Chuma cha uchimo sichithangata;

koma chilungamo chipulumutsa kuimfa.

3 Mas. 34.9-10 Yehova samvetsa njala moyo wa wolungama;

koma amainga chifuniro cha wochimwa.

4Wochita ndi dzanja laulesi amasauka;

koma dzanja la akhama lilemeretsa.

5Wokolola m'malimwe ndi mwana wanzeru;

koma wogona pakututa ndi mwana wochititsa manyazi.

6Madalitso ali pamutu pa wolungama;

koma m'kamwa mwa oipa mubisa chiwawa.

7 Mas. 9.5-6; 112.6 Amayesa wolungama wodala pomkumbukira;

koma dzina la oipa lidzavunda.

8Mwini mtima wanzeru amalandira malamulo;

koma chitsiru cholongolola chidzagwa.

9 Yes. 33.15-16 Woyenda moongoka amayenda osatekeseka;

koma wokhotetsa njira zake adzadziwika.

10Wotsinzinira achititsa chisoni;

koma wodzudzula momveka achita mtendere.

11 Mas. 37.30 M'kamwa mwa wolungama ndi kasupe wa moyo;

koma m'kamwa mwa oipa mubisa chiwawa.

12 1Ako. 13.4; 1Pet. 4.8 Udani upikisanitsa;

koma chikondi chikwirira zolakwa zonse.

13Nzeru ipezedwa m'milomo ya wozindikira;

koma wopusa pamsana pake nthyole.

14Anzeru akundika zomwe adziwa;

koma m'kamwa mwa chitsiru muononga tsopano lino.

15 Mas. 52.7; 1Tim. 6.17 Chuma cha wolemera ndi mzinda wake wolimba;

koma umphawi wao uononga osauka.

16Ntchito za wolungama zipatsa moyo;

koma phindu la oipa lichimwitsa.

17Wosunga mwambo ali m'njira ya moyo;

koma wosiya chidzudzulo asochera.

18 Mas. 15.3 Wobisa udani ali ndi milomo yonama;

wonena ugogodi ndiye chitsiru.

19 Yak. 3.2 Pochuluka mau zolakwa sizisoweka;

koma wokhala chete achita mwanzeru.

20Lilime la wolungama likunga siliva wosankhika;

koma mtima wa oipa uli wachabe.

21Milomo ya wolungama imadyetsa ambiri;

koma zitsiru zimafa posowa nzeru.

22 Gen. 24.35 Madalitso a Yehova alemeretsa,

saonjezerapo chisoni.

23Masewero a chitsiru ndiwo kuchita zoipa;

koma masewero a wozindikira ndiwo nzeru.

24 1Yoh. 5.14-15 Chomwe woipa achiopa chidzamfikira;

koma chomwe olungama achifuna chidzapatsidwa.

25 Mat. 7.24 Monga kavumvulu angopita, momwemo woipa kuli zii;

koma olungama ndiwo maziko osatha.

26Ngati vinyo wowawa m'mano, ndi utsi m'maso,

momwemo waulesi kwa iwo amene amtuma.

27 Mas. 55.23 Kuopa Yehova kutanimphitsa masiku;

koma zaka za oipa zidzafinimpha.

28 Mas. 112.10 Chiyembekezo cha olungama ndicho chimwemwe;

koma chidikiro cha oipa chidzaonongeka.

29Njira ya Yehova ndi linga kwa woongoka mtima;

koma akuchita zoipa adzaonongeka.

30 Mas. 125.1 Wolungama sadzachotsedwa konse;

koma oipa sadzakhalabe m'dziko.

31M'kamwa mwa wolungama mulankhula nzeru;

koma lilime lokhota lidzadulidwa.

32 Mas. 37.30 Milomo ya wolungama idziwa zokondweretsa;

koma m'kamwa mwa oipa munena zokhota.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help