MASALIMO 133 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

Chikondano cha abale ndi chokomaNyimbo yokwerera; ya Davide.

1 Gen. 13.8; Aheb. 13.1 Onani, nkokoma ndi kokondweretsa ndithu

kuti abale akhale pamodzi!

2 Eks. 30.25, 30 Ndiko ngati mafuta a mtengo wake pamutu,

akutsikira kundevu,

inde kundevu za Aroni;

akutsikira kumkawo wa zovala zake.

3 Deut. 28.8 Ngati mame a ku Heremoni,

akutsikira pa mapiri a Ziyoni.

Pakuti pamenepo Yehova analamulira dalitsolo,

ndilo moyo womka muyaya.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help