MASALIMO 84 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

Okhala m'nyumba ya Yehova ndiwo amwaiKwa Mkulu wa Nyimbo: pa Gititi; Salimo la ana a Kora.

1 Mas. 27.4 Pokhala Inu mpotikonda ndithu,

Yehova wa makamu!

2 Mas. 42.1-2 Moyo wanga ulakalaka, inde ukomokanso ndi kufuna mabwalo a Yehova;

mtima wanga ndi thupi langa zifuulira kwa Mulungu wamoyo.

3Mbawanso inapeza nyumba,

ndi namzeze chisa chake choikamo ana ake,

pa maguwa a nsembe anu, Yehova wa makamu,

mfumu yanga ndi Mulungu wanga.

4 Mas. 65.4 Odala iwo akugonera m'nyumba mwanu;

akulemekezani chilemekezere.

5Wodala munthu amene mphamvu yake ili mwa Inu;

mumtima mwake muli makwalala a ku Ziyoni.

6Popyola chigwa cha kulira misozi achiyesa cha akasupe;

inde mvula ya chizimalupsa ichidzaza ndi madalitso.

7 Yob. 17.9 Apita mwamphamvu naonjezapo mphamvu,

aoneka pamaso pa Mulungu mu Ziyoni.

8Yehova Mulungu wa makamu, imvani pemphero langa.

Tcherani khutu, Mulungu wa Yakobo.

9 Gen. 15.1 Onani, Mulungu, ndinu chikopa chathu;

ndipo penyani pa nkhope ya Wodzozedwa wanu.

10Pakuti tsiku limodzi m'mabwalo anu likoma

koposa masiku ambirimbiri akukhala pena.

Kukhala ine wapakhomo m'nyumba ya Mulungu wanga,

kundikonda ine koposa kugonera m'mahema a choipa.

11 Yes. 60.19-20; Mat. 6.33; 7.11 Pakuti Yehova Mulungu ndiye dzuwa ndi chikopa;

Yehova adzapatsa chifundo ndi ulemerero;

sadzakaniza chokoma iwo akuyenda angwiro.

12 Mas. 2.12 Yehova wa makamu,

wodala munthu wakukhulupirira Inu.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help