MASALIMO 124 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

Mulungu yekha walanditsa anthu akeNyimbo yokwerera; ya Davide.

1Akadapanda kukhala nafe Yehova,

anene tsono Israele;

2Akadapanda kukhala nafe Yehova,

pakutiukira anthu:

3 Mas. 56.1-2 Akadatimeza amoyo,

potipsera mtima wao.

4Akadatimiza madziwo,

mtsinje ukadapita pa moyo wathu;

5madzi odzikuza akadapita pa moyo wathu.

6Alemekezedwe Yehova,

amene sanatipereke kumano kwao tikhale chakudya chao.

7 Miy. 6.5 Moyo wathu unaonjoka ngati mbalame mu msampha wa msodzi;

msampha unathyoka ndi ife tinaonjoka.

8 Mas. 121.2; 134.3 Thandizo lathu lili m'dzina la Yehova,

wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help