MASALIMO 72 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

Za ufumu wa Mfumu yokomaSalimo la Solomoni.

1Patsani mfumu maweruzo anu, Mulungu,

ndi mwana wa mfumu chilungamo chanu.

2 Yes. 11.2-4 Potero adzanenera anthu anu mlandu ndi m'chilungamo,

ndi ozunzika anu ndi m'chiweruzo.

3 Yes. 52.7 Mapiri adzatengera anthu mtendere,

timapiri tomwe, m'chilungamo.

4Adzaweruza ozunzika a mwa anthu,

adzapulumutsa ana aumphawi,

nadzaphwanya wosautsa.

5 Mas. 89.36-37 Adzakuopani momwe likhalira dzuwa ndi mwezi,

kufikira mibadwomibadwo.

6 Hos. 6.3 Adzanga mvula yakugwa pa udzu wosenga,

monga mvula yothirira dziko.

7 Yes. 2.4 Masiku ake wolungama adzakhazikika;

ndi mtendere wochuluka, kufikira sipadzakhala mwezi.

8 1Maf. 4.21, 24; Zek. 9.10 Ndipo adzachita ufumu kuchokera kunyanja kufikira kunyanja,

ndi kuchokera ku Mtsinje kufikira malekezero a dziko lapansi.

9 Yes. 49.23 Okhala m'chipululu adzagwadira pamaso pake;

ndi adani ake adzaluma nthaka.

10 Yes. 60.6, 9 Mafumu a ku Tarisisi ndi ku Zisumbuzo adzabwera nacho chopereka;

mafumu a ku Sheba ndi Seba adzadza nazo mphatso.

11 Yes. 49.22-23 Inde mafumu onse adzamgwadira iye,

amitundu onse adzamtumikira.

12 Mas. 35.10 Pakuti adzapulumutsa waumphawi wofuulayo;

ndi wozunzika amene alibe mthandizi.

13Adzachitira nsoni wosauka ndi waumphawi,

nadzapulumutsa moyo wa aumphawi.

14 Mas. 116.15 Adzaombola moyo wao ku chinyengo ndi chiwawa;

ndipo mwazi wao udzakhala wa mtengo pamaso pake.

15Ndipo iye adzakhala ndi moyo;

ndipo adzampatsa golide wa ku Sheba;

nadzampempherera kosalekeza;

adzamlemekeza tsiku lonse.

16M'dzikomo mudzakhala dzinthu dzochuluka

pamwamba pa mapiri;

zipatso zake zidzati waa, ngati za ku Lebanoni,

ndipo iwo a m'mizinda adzaphuka ngati msipu wapansi.

17 Gen. 22.18; Mas. 89.36 Dzina lake lidzakhala kosatha,

momwe likhalira dzuwa dzina lake lidzamvekera zidzukulu.

Ndipo anthu adzadalitsidwa mwa Iye;

amitundu onse adzamutcha wodala.

18 Mas. 77.14 Wolemekezeka Yehova Mulungu, Mulungu wa Israele,

amene achita zodabwitsa yekhayo.

19 Neh. 9.5; Zek. 14.9 Ndipo dzina lake la ulemerero lidalitsike kosatha;

ndipo dziko lonse lapansi lidzale nao ulemerero wake.

Amen, ndi Amen.

20Mapemphero a Davide mwana wa Yese atha.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help