MIYAMBO 5 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

Achenjere naye mkazi woipa

1Mwananga, mvera nzeru yanga;

tcherera makutu ku luntha langa;

2ukasunge zolingalira,

milomo yako ilabadire zomwe udziwa.

3 Miy. 2.16; 6.24 Pakuti milomo ya mkazi wachiwerewere ikukha uchi;

m'kamwa mwake muti see koposa mafuta.

4Chimaliziro chake nchowawa ngati chivumulo,

ndi chakuthwa ngati lupanga lakuthawa konsekonse.

5Mayendedwe ake atsikira kuimfa;

mapazi ake aumirira kumanda;

6sasinkhasinkha bwino za njira ya moyo;

mayendedwe ake adzandira dzandidzandi osadziwa iye.

7Ndipo tsopano ana, mundimvere,

musapatuke ku mau a m'kamwa mwanga.

8Siyanitsa njira yako kutali kwa iyeyo,

osayandikira ku khomo la nyumba yake;

9kuti ungapereke ulemu wako kwa ena,

ndi zaka zako kwa ankhanza;

10kuti mphamvu yako isakhutitse alendo,

ndi kuti usagwire ntchito m'nyumba ya wachilendo;

11ungalire pa chimaliziro chako,

pothera nyama yako ndi thupi lako;

12ndi kuti, Bwanji ndinada mwambo,

mtima wanga ndi kunyoza chidzudzulo;

13ndipo sindinamvere mau a aphunzitsi anga;

ngakhale kutcherera makutu kwa akundilanga mwambo!

14Ndikadakhala m'zoipa zonse,

m'kati mwa msonkhano ndi khamu la anthu.

15Imwa madzi a m'chitsime mwako,

ndi madzi oyenda a m'kasupe mwako.

16Kodi magwero ako ayenera kumwazika kunja,

ndi mitsinje ya madzi m'makwalala?

17Ikhale ya iwe wekha,

si ya alendo okhala nawe ai.

18Adalitsike kasupe wako;

ukondwere ndi mkazi wokula nayo.

19Ngati mbawala yokonda ndi chinkhoma chachisomo,

maere ake akukwanire nthawi zonse;

ukodwe ndi chikondi chake osaleka.

20Pakuti ukondwerenji, mwananga, ndi mkazi wachiwerewere,

ndi kufungatira chifuwa cha mkazi wachilendo?

21 Yer. 16.17; Hos. 7.2 Pakuti njira za munthu zili pamaso pa Yehova,

asinkhasinkha za mayendedwe ake onse.

22 Mas. 9.15 Zoipa zakezake zidzagwira woipa;

adzamangidwa ndi zingwe za uchimo wake.

23Adzafa posowa mwambo;

adzasochera popusa kwambiri.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help