MASALIMO 92 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

Anthu onse ayamike Mulungu chifukwa cha ntchito zake, chilungamo chake, ndi chifundo chakeSalimo, Nyimbo ya pa Sabata.

1 Mas. 96.10; Yes. 51.9 Nkokoma kuyamika Yehova,

ndi kuimbira nyimbo dzina lanu, Wam'mwambamwamba Inu.

2 Mas. 119.147-148 Kuonetsera chifundo chanu mamawa,

ndi chikhulupiriko chanu usiku uliwonse.

3 Mas. 33.2 Pa choimbira cha zingwe khumi ndi pachisakasa;

pazeze ndi kulira kwake.

4Popeza Inu, Yehova, munandikondweretsa ndi kuchita kwanu,

ndidzafuula mokondwera pa ntchito ya manja anu.

5 Aro. 11.33-34 Ha! Ntchito zanu nzazikulu, Yehova,

zolingalira zanu nzozama ndithu.

6Munthu wopulukira sachidziwa;

ndi munthu wopusa sachizindikira ichi;

7 Mas. 37.1-2; 112.10 chakuti pophuka oipa ngati msipu,

ndi popindula ochita zopanda pake;

chitero kuti adzaonongeke kosatha.

8Koma Inu, Yehova, muli m'mwamba kunthawi yonse.

9 Eks. 15.6 Pakuti, taonani, adani anu, Yehova,

pakuti, taonani, adani anu adzatayika;

ochita zopanda pake onse adzamwazika.

10 Mas. 23.5 Koma munakweza nyanga yanga ngati ya njati;

anandidzoza mafuta atsopano.

11Diso langa lapenya chokhumba ine pa iwo ondilalira,

m'makutu mwanga ndamva chokhumba ine

pa iwo akuchita zoipa akundiukira.

12 Mas. 1.3; Hos. 14.5-6 Wolungama adzaphuka ngati mgwalangwa;

adzakula ngati mkungudza wa ku Lebanoni.

13Iwo ookedwa m'nyumba ya Yehova,

adzaphuka m'mabwalo a Mulungu wathu.

14Atakalamba adzapatsanso zipatso;

adzadzazidwa ndi madzi nadzakhala abiriwiri,

15 Deut. 32.4; Aro. 9.14 kulalikira kuti Yehova ngwolunjika;

Iye ndiye thanthwe langa, ndipo mwa Iye mulibe chosalungama.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help