MASALIMO 110 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

Ufumu wa AmbuyeSalimo la Davide.

1 Mat. 22.44; Mrk. 12.36; Luk. 20.42; Mac. 2.34; 1Ako. 15.25; Aheb. 1.13 Yehova ananena kwa Ambuye wanga,

Khalani padzanja lamanja langa,

kufikira nditaika adani anu chopondapo mapazi anu.

2Yehova adzatumiza ndodo ya mphamvu yanu kuchokera ku Ziyoni;

chitani ufumu pakati pa adani anu.

3 Ower. 5.2 Anthu anu adzadzipereka eni ake tsiku la chamuna chanu:

M'moyera mokometsetsa, mobadwira matanda kucha,

muli nao mame a ubwana wanu.

4 Gen. 14.18; Aheb. 5.6 Yehova walumbira, ndipo sadzasintha,

Inu ndinu wansembe kosatha

monga mwa chilongosoko cha Melkizedeki.

5 Mas. 2.5, 12 Ambuye padzanja lamanja lako

adzaphwanya mafumu tsiku la mkwiyo wake.

6Adzaweruza mwa amitundu,

adzadzaza dziko ndi mitembo;

adzaphwanya mitu m'maiko ambiri.

7 Ower. 7.5-6 Adzamwa kumtsinje wa panjira;

chifukwa chake adzaweramutsa mutu wake.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help