1 Rut. 4.11 Mkazi yense wanzeru amanga banja lake;
koma wopusa alipasula ndi manja ake.
2Woyenda moongoka mtima aopa Yehova;
koma wokhota m'njira yake amnyoza.
3M'kamwa mwa chitsiru muli nthyole ya kudzikuza;
koma milomo ya anzeru idzawasunga.
4Popanda zoweta modyera muti see;
koma mphamvu ya ng'ombe ichulukitsa phindu.
5 Eks. 23.1 Mboni yokhulupirika siidzanama;
koma mboni yonyenga imalankhula zonama.
6Wonyoza afunafuna nzeru osaipeza;
koma wozindikira saona vuto m'kuphunzira.
7Pita pamaso pa munthu wopusa,
sudzazindikira milomo yakudziwa.
8Nzeru ya wochenjera ndiyo yakuti azindikire njira yake;
koma utsiru wa opusa ndiwo chinyengo.
9Zitsiru zinyoza kupalamula;
koma mwa oongoka mtima muli chiyanjano.
10Mtima udziwa kuwawa kwakekwake;
mlendo sadudukira ndi chimwemwe chake.
11 Yob. 8.15 Nyumba ya oipa idzapasuka;
koma hema wa oongoka mtima adzakula.
12 Aro. 6.21 Ilipo njira yooneka kwa mwamuna ngati yoongoka;
koma matsiriziro ake ndi njira za imfa.
13Ngakhale m'kuseka mtima uwawa;
ndipo matsiriziro a chiphwete ndi chisoni.
14Wobwerera m'mbuyo m'mtima adzakhuta njira yake;
koma munthu wabwino adzakhuta za mwa iye yekha.
15Wachibwana akhulupirira mau onse;
koma wochenjera asamalira mayendedwe ake.
16Wanzeru amaopa nasiya zoipa;
koma wopusa amanyada osatekeseka.
17Wokangaza kukwiya adzachita utsiru;
ndipo munthu wa ziwembu adzadedwa.
18Achibwana amalandira cholowa cha utsiru;
koma ochenjera amavala nzeru ngati korona.
19Oipa amagwadira abwino,
ndi ochimwa pa makomo a olungama.
20Waumphawi adedwa ndi anzake omwe;
koma akukonda wolemera achuluka.
21 Mas. 41.1 Wonyoza anzake achimwa;
koma wochitira osauka chifundo adala.
22Kodi oganizira zoipa sasochera?
Koma akuganizira zabwino adzalandira chifundo ndi ntheradi.
23M'ntchito zonse muli phindu;
koma kulankhulalankhula kungopatsa umphawi.
24Korona wa anzeru ndi chuma chao;
utsiru wa opusa ndiwo utsiru.
25Mboni yoona imalanditsa miyoyo;
koma wolankhula zonama angonyenga.
26Wakuopa Yehova akhulupirira kolimba;
ndipo ana ake adzakhala ndi pothawirapo.
27Kuopa Yehova ndiko kasupe wa moyo,
kupatutsa kumisampha ya imfa.
28Mu unyinji wa anthu muli ulemu wa mfumu;
koma popanda anthu kalonga aonongeka.
29 Yak. 1.19 Wosakwiya msanga apambana kumvetsa;
koma wansontho akuza utsiru.
30Mtima wabwino ndi moyo wa thupi;
koma nsanje ivunditsa mafupa.
31 Mat. 25.40, 45 Wotsendereza aumphawi atonza Mlengi wake;
koma wochitira wosauka chifundo amlemekeza.
32 Mas. 23.4; 2Ako. 5.8; 2Tim. 4.18 Wochimwa adzakankhidwa m'kuipa kwake;
koma wolungama akhulupirirabe pomwalira.
33Nzeru ikhalabe m'mtima wa wozindikira,
nidziwika pakati pa opusa.
34Chilungamo chikuza mtundu wa anthu;
koma tchimo lichititsa fuko manyazi.
35 Mat. 24.45, 47 Mfumu ikomera mtima kapolo wochita mwanzeru;
koma idzakwiyira wochititsa manyazi.
Who We AreWhat We EelieveWhat We Do
2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.