1Wolemekezeka Yehova thanthwe langa,
wakuphunzitsa manja anga achite nkhondo,
zala zanga zigwirane nao:
2 2Sam. 22.2-3, 40, 48 Ndiye chifundo changa, ndi linga langa,
msanje wanga, ndi Mpulumutsi wanga;
chikopa changa, ndi Iye amene ndimtama;
amene andigonjetsera anthu anga.
3 Mas. 8.4; Aheb. 2.6 Yehova, munthu ndani kuti mumdziwa?
Mwana wa munthu kuti mumsamalira?
4 Mas. 102.11 Munthu akunga mpweya;
masiku ake akunga mthunzi wopitirira.
5 Yes. 64.1 Weramutsani thambo lanu, Yehova, nimutsike:
Khudzani mapiri ndipo adzafuka.
6Ng'animitsani mphezi, ndi kuwabalalitsa;
tumizani mivi yanu, ndi kuwapirikitsa.
7 Mas. 18.16 Tulutsani manja anu kuchokera m'mwamba;
ndikwatuleni ndi kundilanditsa kumadzi aakulu,
kudzanja la alendo;
8amene pakamwa pao alankhula zachabe,
ndi dzanja lao lamanja ndilo dzanja lachinyengo.
9 Mas. 33.2-3 Ndidzakuimbirani nyimbo yatsopano, Mulungu;
pa chisakasa cha zingwe khumi ndidzaimbira zakukulemekezani.
10 Mas. 18.50 Ndiye amene apatsa mafumu chipulumutso:
Amene alanditsa Davide mtumiki wake kulupanga loipa.
11Ndilanditseni ndi kundipulumutsa kudzanja la alendo,
amene pakamwa pao alankhula zachabe,
ndi dzanja lao lamanja ndilo dzanja lachinyengo.
12 Mas. 128.3; 1Pet. 3.5 Kuti ana athu aamuna akhale ngati mmera udakula usanakhwime;
ana athu aakazi ngati nsanamira za kungodya,
zosema zikometsere nyumba ya mfumu.
13Kuti nkhokwe zathu zidzale, kutipatsa za mitundumitundu;
ndi kuti nkhosa zathu ziswane zikwizikwi, inde zikwi khumi kubusako.
14Kuti ng'ombe zathu zikhale zosenza katundu;
ndi kuti pasakhale kupasula linga kapena kutulukamo,
pasakhalenso kufuula m'makwalala athu.
15 Deut. 33.29 Odala anthu akuona zotere;
odala anthu amene Mulungu wao ndi Yehova.
Who We AreWhat We EelieveWhat We Do
2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.