1 Miy. 4.14-15; Mas. 26.4 Wodala munthuyo wosayenda mu uphungu wa oipa,
kapena wosaimirira m'njira ya ochimwa,
kapena wosakhala pansi pa bwalo la onyoza.
2 Mas. 119.35, 47, 92, 97 Komatu m'chilamulo cha Yehova muli chikondwerero chake;
ndipo m'chilamulo chake amalingirira usana ndi usiku.
3 Yer. 17.8 Ndiye akunga mtengo wooka pa mitsinje ya madzi;
wakupatsa chipatso chake pa nyengo yake,
tsamba lake lomwe losafota;
ndipo zonse azichita apindula nazo.
4 Yes. 17.13 Oipa satero ai;
koma akunga mungu wouluka ndi mphepo.
5Chifukwa chake oipa sadzaimirira pa mlanduwo,
kapena ochimwa mu msonkhano wa olungama.
6 Nah. 1.7; 2Tim. 2.19 Pakuti Yehova adziwa mayendedwe a olungama;
koma mayendedwe a oipa adzatayika.
Who We AreWhat We EelieveWhat We Do
2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.