MASALIMO 128 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

Wakuopa Yehova adalitsidwa m'banja mwakeNyimbo yokwerera.

1 Mas. 119.1 Wodala yense wakuopa Yehova,

wakuyenda m'njira zake.

2 Yes. 3.10 Pakuti udzadya za ntchito ya manja ako;

wodala iwe, ndipo kudzakukomera.

3 Mas. 52.8; Ezk. 19.10 Mkazi wako adzanga mpesa wopatsa m'mbali za nyumba yako;

ana ako adzanga timitengo ta azitona pozinga podyera pako.

4Taonani, m'mwemo adzadalitsika

munthu wakuopa Yehova.

5Yehova adzakudalitsa ali mu Ziyoni;

ndipo udzaona zokoma za Yerusalemu masiku onse a moyo wako.

6 Gen. 50.23 Inde, udzaona zidzukulu zako.

Mtendere ukhale ndi Israele.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help