MASALIMO 121 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

Mulungu Msungi wokhulupirika wa anthu akeNyimbo yokwerera.

1Ndikweza maso anga kumapiri:

Thandizo langa lidzera kuti?

2 Mas. 124.8 Thandizo langa lidzera kwa Yehova,

wakulenga kumwamba ndi dziko lapansi.

3 1Sam. 2.9; Yes. 27.3 Sadzalola phazi lako literereke:

Iye amene akusunga sadzaodzera.

4Taonani, wakusunga Israele

sadzaodzera kapena kugona.

5 Yes. 25.4 Yehova ndiye wakukusunga;

Yehova ndiye mthunzi wako wa kudzanja lako lamanja.

6 Yes. 49.10 Dzuwa silidzawamba usana,

mwezi sudzakupanda usiku.

7 Mas. 97.10 Yehova adzakusunga kukuchotsera zoipa zilizonse;

adzasunga moyo wako.

8 Deut. 28.6 Yehova adzasungira kutuluka kwako ndi kulowa kwako,

kuyambira tsopano kufikira nthawi zonse.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help