1 1Maf. 4.32; Mlal. 12.9 Miyambo ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israele.
2Kudziwa nzeru ndi mwambo;
kuzindikira mau ozindikiritsa;
3kulandira mwambo wakusamalira machitidwe,
chilungamo, chiweruzo ndi zolunjika;
4kuchenjeza achibwana,
kuphunzitsa mnyamata kudziwa ndi kulingalira;
5 Miy. 9.9 kuti wanzeru amve, naonjezere kuphunzira;
ndi kuti wozindikira afikire kuuphungu;
6kuzindikira mwambi ndi tanthauzo lake,
mau a anzeru, ndi zophiphiritsa zao.
Munthu asalole oipa amchete7 Miy. 9.10 Kuopa Yehova ndiko chiyambi cha kudziwa;
opusa anyoza nzeru ndi mwambo.
8 Aef. 6.1, 2 Mwananga, tamva mwambo wa atate wako,
ndi kusasiya chilangizo cha amai ako;
9pakuti izi ndi korona wa chisomo pamutu pako,
ndi mkanda pakhosi pako.
10 Gen. 39.7-8 Mwananga, akakukopa ochimwa usalole.
11 Yes. 5.26 Akanena, Idza nafe, tibisalire mwazi,
tilalire osachimwa opanda chifukwa;
12tiwameze ali ndi moyo ngati manda,
ali amphumphu, ngati akutsikira kudzenje;
13tidzapeza chuma chonse cha mtengo wake,
tidzadzaza nyumba zathu ndi zofunkha;
14udzachita nafe maere,
tonse tidzakhala ndi chotengeramo chimodzi.
15 Mas. 1.1 Mwananga, usayende nao m'njira;
letsa phazi lako ku mayendedwe ao;
16 Yes. 59.7 pakuti mapazi ao athamangira zoipa,
afulumira kukhetsa mwazi.
17Pakuti kutchera msampha pamaso pa mbalame ndi chabe;
18ndipo awa abisalira mwazi waowao, alalira miyoyo yaoyao.
19 1Tim. 6.10 Mayendedwe a yense wopindula chuma monyenga ngotere;
chilanda moyo wa eni ake.
Chenjezo la Nzeru20Nzeru ifuula panja;
imveketsa mau ake pabwalo;
21iitana posonkhana anthu polowera pachipata;
m'mzinda inena mau ake,
22Kodi mudzakonda zazibwana kufikira liti, achibwana inu?
Onyoza ndi kukonda kunyoza,
opusa ndi kuda nzeru?
23 Yow. 2.28 Tembenukani pamene ndikudzudzulani;
taonani, nditsanulira pa inu mzimu wanga,
ndikudziwitsani mau anga.
24 Yes. 66.4 Chifukwa ndaitana, ndipo munakana;
ndatambasula dzanja langa,
ndipo panalibe analabadira;
25 Luk. 7.30 koma munapeputsa uphungu wanga wonse,
ndi kukana kudzudzula kwanga.
26 Mas. 2.4 Inetu ndidzachitira chiphwete tsoka lanu,
ndidzatonyola pakudza mantha anu;
27pakudza mantha anu ngati mphepo yopasula,
ndi pofika tsoka lanu ngati kamvulumvulu;
pakudza kwa inu vuto ndi nsautso.
28 Yer. 11.11; Yak. 4.3 Pamenepo adzandiitana,
koma sindidzavomera;
adzandifunatu, osandipeza ai;
29 Mas. 119.173 chifukwa anada nzeru,
sanafune kuopa Yehova;
30anakana uphungu wanga,
nanyoza kudzudzula kwanga konse;
31 Yes. 3.11; Agal. 6.7 momwemo adzadya zipatso za mayendedwe ao,
nadzakhuta zolingalira zao.
32Pakuti kubwerera m'mbuyo kwa achibwana kudzawapha;
ndipo mphwai za opusa zidzawaononga.
33 Mas. 25.12-13 Koma wondimvera ine adzakhala osatekeseka,
nadzakhala phee osaopa zoipa.
Who We AreWhat We EelieveWhat We Do
2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.