MASALIMO 10 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

Athamangira Mulungu pothawa adani omtsata

1Muimiranji patali, Yehova?

Mubisaliranji m'nyengo za nsautso?

2 Mas. 7.16 Podzikuza woipa apsereza waumphawi;

agwe m'chiwembu anapanganacho.

3 Mas. 94.4 Pakuti woipa adzitamira chifuniro cha moyo wake,

adalitsa wosirira, koma anyoza Yehova.

4 Mas. 14.2 Woipa, monga mwa kudzikuza kwa nkhope yake, akuti, Sadzafunsira.

Malingaliro ake onse akuti, Palibe Mulungu.

5Mayendedwe ake alimbika nthawi zonse;

maweruzo anu ali pamwamba posaona iye;

adani ake onse awanyodola.

6Ati mumtima mwake, Sindidzagwedezeka ine;

ku mibadwomibadwo osagwa m'tsoka ine.

7 Mas. 12.2 M'kamwa mwake mwadzala kutemberera

ndi manyengo ndi kuchenjerera;

pansi pa lilime lake pali chivutitso chopanda pake.

8 Mas. 17.11, 12 Akhala m'molalira midzi;

mobisalamo akupha munthu wosachimwa.

Ambisira waumphawi nkhope yake.

9Alalira monga mkango m'ngaka mwake;

alalira kugwira wozunzika,

agwira wozunzika, pakumkola mu ukonde mwake.

10Aunthama, nawerama,

ndipo aumphawi agwa m'zala zake.

11Anena m'mtima mwake, Mulungu waiwala;

wabisa nkhope yake; sapenya nthawi zonse.

12Ukani, Yehova; samulani dzanja lanu, Mulungu;

musaiwale ozunzika.

13Woipa anyozeranji Mulungu,

anena m'mtima mwake, Simudzafunsira?

14 Mas. 68.5; 2Tim. 1.12 Mwapenya; pakuti mumayang'anira chivutitso

ndi chisoni kuti achipereke m'manja mwanu;

waumphawi adzipereka kwa Inu;

wamasiye mumakhala mthandizi wake.

15 Mas. 37.17 Thyolani mkono wa woipa;

ndipo wochimwa, mutsate choipa chake

kufikira simuchipezanso china.

16 Yer. 10.10 Yehova ndiye Mfumu kunthawi yamuyaya;

aonongeka amitundu m'dziko lake.

17Yehova, mwamva chikhumbo cha ozunzika,

mudzakhazikitsa mtima wao, mudzatchereza khutu lanu;

18 Yes. 1.17 kuti muweruze mlandu wa amasiye ndi wokhalira mphanthi,

kuti munthu wa padziko lapansi angaonjeze kuopsa.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help