MASALIMO 11 - Buku Lopatulika ndilo Mau a Mulungu

Yehova asunga anthu ake nalanga oipaKwa Mkulu wa Nyimbo. Salimo la Davide.

1 1Sam. 26.20; Mas. 56.11 Ndakhulupirira Yehova,

mutani nkunena kwa moyo wanga,

Thawirani kuphiri lanu ngati mbalame?

2Pakuti, onani, oipa akoka uta,

apiringidza muvi wao pansinga,

kuwaponyera mumdima oongoka mtima.

3Akapasuka maziko,

wolungama angachitenji?

4 Mas. 33.13-14; Yes. 66.1; Hab. 2.20 Yehova ali mu Kachisi wake woyera,

Yehova, mpando wachifumu wake uli mu Mwamba;

apenyerera ndi maso ake, ayesa ana a anthu ndi zikope zake.

5 Gen. 22.1; Yak. 1.12 Yehova ayesa wolungama mtima,

koma moyo wake umuda woipa ndi iye wakukonda chiwawa.

6 Ezk. 38.22 Adzagwetsa pwatapwata misampha pa oipa;

moto ndi miyala ya sulufure,

ndi mphepo yoopsa zidzawagawikira m'chikho chao.

7 Mas. 45.7; 1Yoh. 3.2 Pakuti Yehova ndiye wolungama; akonda zolungama;

woongoka mtima adzapenya nkhope yake.

Blog
About Us
Message
Site Map

Who We AreWhat We EelieveWhat We Do

Terms of UsePrivacy Notice

2025 by iamachristian.org,Inc All rights reserved.

Home
Gospel
Question
Blog
Help